< Psaumes 43 >

1 Rends-moi justice, ô Dieu, et prends en main ma cause contre un peuple sans piété; délivre-moi de gens perfides et iniques;
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 car tu es mon Dieu, ma forteresse. Pourquoi m’as-tu délaissé? Pourquoi marché-je, voilé de tristesse, sous l’oppression de l’ennemi?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Envoie ta lumière et ta vérité: qu’elles soient mes guides, qu’elles me conduisent à ta montagne sainte, dans ta demeure!
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Je voudrais revenir auprès de l’autel de Dieu, du Dieu qui est ma joie et mon bonheur; je voudrais te louer avec la harpe, ô Dieu, mon Dieu!
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Pourquoi es-tu affaissée, mon âme? Pourquoi t’agites-tu dans mon sein? Mets ton espoir en Dieu, car j’aurai encore à le louer, lui, mon sauveur et mon Dieu!
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

< Psaumes 43 >