< Psaumes 28 >

1 De David. C’Est vers toi que je crie, ô Seigneur! Mon Rocher, ne m’oppose pas ton silence, car si tu gardais le silence à mon égard, je serais pareil à ceux qui descendent au tombeau.
Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2 Ecoute ma voix suppliante quand je t’invoque, quand j’élève les mains vers ton auguste sanctuaire.
Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3 Ne me confonds pas avec les méchants, avec les artisans d’iniquité, qui parlent paix à leurs proches, et n’ont que méchanceté au cœur.
Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4 Donne-leur le prix de leur conduite, de leurs actes pervers, traite-les selon l’œuvre de leurs mains; paie-leur le salaire qu’ils méritent.
Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5 Car ils ne prêtent aucune attention aux actes de l’Eternel, ni à l’œuvre de ses mains: qu’il les renverse pour ne plus les relever!
Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
6 Béni soit le Seigneur, car il a entendu ma voix suppliante!
Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7 L’Eternel est ma force, mon bouclier; en lui mon cœur s’est confié et j’ai été secouru. Aussi mon cœur est-il en joie. Par mon cantique, je vais lui rendre grâce.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8 L’Eternel est une force pour son peuple, un rempart protecteur pour son oint.
Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9 Prête assistance à ton peuple et bénis ton héritage: conduis-les comme un berger et soutiens-les jusque dans l’éternité.
Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

< Psaumes 28 >