< Psaumes 17 >

1 Prière de David. Ecoute, ô Seigneur, ma juste demande, exauce ma supplication, prête l’oreille à ma prière, sortant de lèvres non trompeuses.
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 C’Est de toi qu’émanera mon bon droit: tes yeux discernent ce qui est équitable.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Tu sondes mon cœur, tu m’examines pendant la nuit, tu me mets à l’épreuve, sans trouver en moi aucune pensée qui ne doive passer par ma bouche.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 Guidé par les paroles de tes lèvres, j’observe les actions des hommes, les voies des gens violents.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 Affermis mes pas dans tes sentiers, pour que mes pieds ne glissent point.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 Je t’appelle, car tu me réponds, ô Dieu! Prête-moi l’oreille, entends mes paroles.
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Mets en relief tes bienfaits, ô Protecteur de ceux qui se confient à ta droite, malgré les adversaires.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Garde-moi comme la prunelle des yeux, abrite-moi à l’ombre de tes ailes,
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 contre les méchants qui me tyrannisent, contre mes ennemis qui me cernent avec passion.
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 De leur graisse ils ont bouché leur cœur; leurs lèvres s’expriment avec orgueil.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 A chacun de nos pas, les voilà qui se pressent autour de nous; ils ont les yeux sur nous pour nous étendre à terre,
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 pareils au lion avide de déchirer, au lionceau qui se tient en embuscade.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Lève-toi, Seigneur, préviens ses desseins, fais-lui ployer le genou; par ton glaive, sauve ma vie du méchant.
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 Par ta main, ô Eternel, sauve-moi de ces gens, de ces gens esclaves du monde, qui jouissent largement de la vie, dont tu bourres le ventre de tes biens, dont les enfants ont tout en abondance et laissent leur superflu à leur progéniture.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 Quant à moi, puissé-je, grâce à ma droiture, contempler ta face et, à mon réveil, me rassasier de ta vue!
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

< Psaumes 17 >