< Psaumes 109 >

1 Au chef des chantres. De David. Psaume. Dieu, objet de mes louanges, ne garde pas le silence!
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 Car la bouche du méchant, la bouche de la fourberie s’ouvrent contre moi; on me parle un langage mensonger.
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 On m’enveloppe de propos haineux, on me fait la guerre sans motif.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 En échange de mon amour, on me traite en ennemi, et moi je ne suis que prière.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 On me rend le mal pour le bien, la haine est le prix de mon affection.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Suscite un méchant contre lui, qu’un accusateur se dresse à sa droite!
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Quand il passe en jugement, qu’il s’en revienne condamné! Que sa prière lui soit imputée à péché!
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Que ses jours soient peu nombreux, qu’un autre s’empare de son office!
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Que ses enfants soient orphelins, que sa femme devienne veuve.
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Que ses enfants errent de tous côtés pour mendier, qu’ils sollicitent, éloignés des ruines de leur demeure.
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Que le créancier saisisse tout son avoir, que des étrangers mettent au pillage le fruit de son labeur.
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Qu’il n’y ait personne pour lui tendre une main secourable, personne pour avoir compassion de ses orphelins.
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Que sa postérité soit condamnée à disparaître, qu’à la génération prochaine son nom soit éteint.
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Que l’iniquité de ses pères soit présente au souvenir de l’Eternel. Que jamais ne s’efface la faute de sa mère.
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Que le Seigneur les ait toujours sous les yeux, et extirpe leur mémoire de la terre;
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 parce qu’il n’a pas songé à pratiquer la charité, qu’il a persécuté un homme malheureux, déshérité, au cœur brisé pour amener sa perte.
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Il a aimé la malédiction: elle est venue le frapper; il n’avait aucun goût pour la bénédiction: elle l’a fui.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Il a endossé la malédiction comme sa tunique; elle a pénétré en son sein comme de l’eau, comme de l’huile dans ses membres.
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Qu’elle soit donc pour lui comme un vêtement dont il s’enveloppe, qu’elle l’entoure comme d’une perpétuelle ceinture.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Que tel soit, de par l’Eternel, le salaire de mes adversaires, de ceux qui débitent des méchancetés contre moi!
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Mais toi, Eternel, Seigneur, traite-moi comme l’exige l’honneur de ton nom, car précieuse est ta grâce: sauve-moi!
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Je suis, en effet, pauvre et misérable, et mon cœur est déchiré en moi.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Pareil à l’ombre qui s’allonge, je m’évanouis, je suis pourchassé comme par une nuée de sauterelles.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Mes genoux flageolent, épuisés par le jeûne; mon corps est amaigri, a perdu toute graisse.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Et je suis devenu pour eux un objet d’opprobre, ils me regardent et hochent la tête.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Secours-moi, Eternel, mon Dieu, accorde-moi ton aide en raison de ta bonté.
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Qu’on sache que cela vient de ta main, que toi, ô Seigneur, tu as tout fait.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Qu’ils maudissent, eux, toi, tu béniras; qu’ils se lèvent, ils seront couverts de honte, et ton serviteur sera dans la joie.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Que mes adversaires se revêtent d’ignominie, qu’ils soient enveloppés de leur honte comme d’un manteau.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Ma bouche abondera en actions de grâce à l’Eternel; au milieu des foules, je proclamerai ses louanges.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 Car il se tient à la droite du malheureux, pour l’assister contre ceux qui condamnent sa personne.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

< Psaumes 109 >