< Proverbes 3 >
1 Mon fils, n’oublie pas mon enseignement; que ton cœur retienne mes recommandations.
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Car ils te vaudront de longs jours, des années de vie et de paix.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Que la bonté et la vérité ne te quittent jamais: attache-les à ton cou, inscris-les sur les tablettes de ton cœur,
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 et tu trouveras faveur et bon vouloir aux yeux de Dieu et des hommes.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Confie-toi en l’Eternel de tout cœur, mais ne te repose pas sur ton intelligence.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Dans toutes tes voies, songe à lui, et il aplanira ta route.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Ne te prends pas pour un sage: crains l’Eternel et fuis le mal;
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 ce sera la santé pour ton corps; une sève généreuse pour tes membres.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honore l’Eternel avec tes biens, avec les prémices de tous tes produits;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 alors tes celliers regorgeront d’abondance et tes pressoirs déborderont de vin.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Ne rejette pas l’admonestation de l’Eternel, ne t’insurge pas contre sa réprimande;
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 car celui qu’il aime, l’Eternel le châtie, tel un père le fils qui lui est cher.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Heureux l’homme qui a atteint la sagesse, le mortel qui met en œuvre la raison!
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Car le trafic en vaut plus que celui de l’argent, et les fruits qu’elle donne l’emportent sur l’or fin.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Elle est plus précieuse que les perles, tes plus chers trésors ne la valent point.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Elle porte la longévité en sa droite, et en sa gauche la richesse et l’honneur.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Ses voies sont des voies pleines de délices, et tous ses sentiers aboutissent au bonheur.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Elle est un arbre de vie pour ceux qui s’en rendent maîtres: s’y attacher, c’est s’assurer la félicité.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 L’Eternel, par la sagesse, a fondé la terre; par l’intelligence, il a affermi les cieux.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Par sa science, les abîmes s’entrouvrent, et les nuées ruissellent de rosée.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Mon fils, ne les laisse pas s’éclipser à tes yeux, reste fidèle à la vérité, et à la réflexion.
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 Elles seront un gage de vie pour ton âme, un ornement gracieux pour ton cou.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Dès lors, tu suivras en sécurité ta route, et ton pied ne bronchera pas.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Lorsque tu te livreras au repos, tu n’éprouveras aucune crainte, tu te coucheras et goûteras un doux sommeil.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Tu ne seras pas exposé à des terreurs soudaines ni au malheur qui fond sur le méchant.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Car l’Eternel sera l’objet de ton espoir; il préservera ton pied des embûches.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Ne refuse pas un bienfait à ceux qui y ont droit, alors qu’il est en ton pouvoir de l’accorder.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Ne dis pas à ton prochain: "Va, tu reviendras; demain je donnerai", quand tu as de quoi.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Ne médite pas de mal contre ton prochain, tandis qu’il demeure sans défiance auprès de toi.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Ne cherche pas de vaine querelle à l’homme qui ne t’a fait aucun rital.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Ne porte envie à aucun homme injuste et n’adopte aucun de ses procédés.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Car l’Eternel a en horreur les gens tortueux, mais les justes jouissent de son intimité.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 La malédiction de l’Eternel repose sur la maison du méchant, mais la demeure du juste est bénie.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Se trouve-t-il en présence de railleurs, il leur oppose la raillerie, mais il accorde sa bienveillance aux humbles.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 L’Honneur sera le lot des sages, mais les sots seront mis en vedette par leur honte.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.