< Proverbes 16 >

1 L’Homme est maître des résolutions de son cœur; mais c’est l’Eternel qui prononce sur elles.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Toutes les voies de l’homme sont pures à ses yeux, mais l’Eternel sonde les esprits.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Remets le succès de tes œuvres à l’Eternel, et tes projets s’en trouveront affermis.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 L’Eternel a tout fait pour un but prédestiné, même le méchant pour le jour du malheur.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Tout cœur hautain est en horreur à l’Eternel: haut la main! il ne restera pas indemne.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 La bonté et la bienveillance effacent la faute; la crainte de l’Eternel fait éviter le mal.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Dieu agrée-t-il les voies d’un homme, il lui concilie même la faveur de ses ennemis.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Mieux vaut une honnête médiocrité qu’un grand revenu, acquis par l’improbité.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Le cœur de l’homme choisit sa voie; mais l’Eternel dirige ses pas.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Ce sont des oracles qui émanent des lèvres du roi: quand il rend la justice, sa bouche ne faillit pas.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Les plateaux, les balances exactes sont choses de Dieu, il est l’auteur de tous les justes poids.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Faire le mal est chose odieuse aux rois; car les trônes s’affermissent par la justice.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Des lèvres loyales font plaisir aux rois; ils aiment qui parle avec droiture.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 Le courroux du roi est un messager de mort, un homme sage sait l’apaiser.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 Que le visage du roi s’éclaire, c’est un gage de vie; sa faveur est comme une nuée chargée de pluie printanière.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Acquérir la sagesse, combien cela est plus précieux que l’or fin! S’Enrichir en sagacité vaut mieux que l’argent.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 La route des justes les éloigne du mal; qui suit droit son chemin préserve sa vie.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 L’Orgueil précède la ruine, l’arrogance est le signe avant-coureur de la chute.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Prendre une attitude modeste avec les humbles vaut mieux que partager du butin avec les orgueilleux.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Qui réfléchit mûrement à une affaire s’assure des avantages; mais heureux qui met sa confiance en l’Eternel!
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 Qui a le cœur sage mérite d’être appelé intelligent; la douceur des lèvres augmente la force de persuasion.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 L’Intelligence est une source de vie pour celui qui en est doué; le châtiment des sots, c’est leur sottise.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Le cœur du sage inspire sa bouche, et augmente la force de persuasion de ses lèvres.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Des paroles amènes sont un rayon de miel, doux à l’âme, bienfaisant au corps.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Tel chemin paraît tout uni à l’homme, et il aboutit aux avenues de la mort.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 C’Est pour lui-même que travaille le laborieux, car pressantes sont les exigences de sa bouche.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 L’Homme sans valeur morale est un artisan de malheur; sur ses lèvres il y a comme un feu dévorant.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 L’Homme artificieux déchaîne la discorde; le boutefeu sème la division entre amis.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 L’Homme violent circonvient son prochain et le mène dans une mauvaise voie.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Il ferme les yeux pour méditer de mauvais coups; il se pince les lèvres: il a consommé le mal!
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 La haute vieillesse est une couronne d’honneur; c’est sur le chemin de la vertu qu’elle se rencontre.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Qui résiste à la colère l’emporte sur le héros; qui domine ses passionssur un preneur de villes.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 On agite le sort dans l’urne mais l’arrêt qu’il prononce vient de l’Eternel.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbes 16 >