< Nombres 36 >

1 Les chefs de famille de la descendance de Ghilad, fils de Makhir, fils de Manassé, de la lignée des enfants de Joseph, se présentèrent et parlèrent ainsi devant Moïse et devant les phylarques, principaux chefs des enfants d’Israël;
Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
2 ils dirent: "L’Éternel a ordonné à mon seigneur d’attribuer le pays en héritage, par la voie du sort, aux enfants d’Israël; d’autre part, mon seigneur a été chargé par l’Éternel d’attribuer l’héritage de Celofhad, notre frère, à ses filles.
Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
3 Or, si elles contractent mariage dans quelqu’une des autres tribus des enfants d’Israël, leur héritage sera retranché de l’héritage de nos pères, s’ajoutera à l’héritage de la tribu où elles auront passé, et notre lot patrimonial en sera amoindri.
Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
4 Lors même que le jubilé aura lieu pour les enfants d’Israël, leur héritage à elles restera joint à celui de la tribu où elles auront passé, et le patrimoine de la tribu de nos pères en restera diminué d’autant."
Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
5 Et Moïse donna aux enfants d’Israël, sur l’ordre de l’Éternel, les instructions suivantes: "La tribu des enfants de Joseph a raison.
Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
6 Voici ce que l’Éternel a prescrit au sujet des filles de Celofhad: elles pourront épouser qui bon leur semblera; toutefois, c’est dans une famille de leur tribu paternelle qu’elles doivent contracter mariage.
Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
7 De la sorte, aucun héritage, chez les enfants d’Israël, ne sera transporté d’une tribu à une autre, mais chacun des enfants d’Israël demeurera attaché à l’héritage de la tribu de ses pères.
kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
8 Toute fille appelée à hériter, parmi les tribus des enfants d’Israël, devra épouser quelqu’un qui appartienne à la tribu de son père; afin que les enfants d’Israël possèdent chacun l’héritage de leurs pères,
Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
9 et qu’il n’y ait pas d’évolution d’héritage d’une tribu à une tribu différente, les tribus des enfants d’Israël devant, chacune, conserver leur héritage."
Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
10 Comme l’Éternel l’avait ordonné à Moïse, ainsi agirent les filles de Celofhad.
Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
11 Mahla, Tirça, Hogla, Milka et Noa se marièrent avec les fils de leurs oncles.
Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
12 Ce fut donc dans les familles issues de Manassé, fils de Joseph, qu’elles se marièrent, et leur héritage resta dans la tribu de leur souche paternelle.
Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
13 Tels sont les préceptes et les statuts que l’Éternel imposa, par l’organe de Moïse, aux enfants d’Israël, dans les plaines de Moab, au bord du Jourdain vers Jéricho.
Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.

< Nombres 36 >