< Nombres 1 >
1 L’Éternel parla en ces termes à Moïse, dans le désert de Sinaï, dans la tente d’assignation, le premier jour du second mois de la deuxième année après leur sortie du pays d’Egypte:
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 "Faites le relevé de toute la communauté des enfants d’Israël, selon leurs familles et leurs maisons paternelles, au moyen d’un recensement nominal de tous les mâles, comptés par tête.
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 Depuis l’âge de vingt ans et au-delà, tous les Israélites aptes au service, vous les classerez selon leurs légions, toi et Aaron.
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 Vous vous adjoindrez un homme par tribu, un homme qui soit chef de sa famille paternelle.
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 Or, voici les noms des hommes qui vous assisteront: pour la tribu de Ruben, Eliçour, fils de Chedéour;
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 pour Siméon, Cheloumïel, fils de Çourichaddaï;
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 pour Juda, Nahchôn, fils d’Amminadab;
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 pour Issachar, Nethanel, fils de Çouar;
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 pour Zabulon, Elïab, fils de Hêlôn;
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 pour les fils de Joseph: pour Ephraïm, Elichama, fils d’Ammihoud; pour Manassé, Gamliel, fils de Pedahçour;
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 pour Benjamin, Abidân, fils de Ghidoni;
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 pour Dan, Ahïézer, fils d’Ammichaddaï;
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 pour Aser, Paghïel, fils d’Okrân;
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 pour Gad, Elyaçaf, fils de Deouêl;
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 pour Nephtali, Ahira, fils d’Enân.
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 Ceux-là sont les élus de la communauté, princes de leurs tribus paternelles; ce sont les chefs des familles d’Israël."
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 Moïse et Aaron s’adjoignirent ces hommes, désignés par leurs noms.
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 Puis ils convoquèrent toute la communauté, le premier jour du second mois; et on les enregistra selon leurs familles et leurs maisons paternelles, en comptant par noms ceux qui avaient vingt ans et plus, chacun individuellement,
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 ainsi que l’Éternel l’avait prescrit à Moïse. Leur dénombrement eut lieu dans le désert de Sinaï.
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 Les descendants de Ruben, premier-né d’Israël, étant classés selon leur origine, leurs familles, leurs maisons paternelles: d’après le compte nominal et par tête, pour tout mâle âgé de vingt ans et plus, apte au service,
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 les recensés, dans la tribu de Ruben, se montèrent à quarante-six mille cinq cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 Pour les descendants de Siméon, classés selon leur origine, leurs familles, leurs maisons paternelles, recensés d’après le compte nominal et par tête de tout mâle âgé de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 les recensés, dans la tribu de Siméon, se montèrent à cinquante-neuf mille trois cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 Pour les descendants de Gad, classés selon leur origine, leurs familles, leurs maisons paternelles: d’après le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 les recensés, dans la tribu de Gad, se montèrent à quarante-cinq mille six cent cinquante.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 Pour les descendants de Juda, classés selon leur origine, leurs familles, leurs maisons paternelles: d’après le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 les recensés, dans la tribu de Juda, se montèrent à soixante-quatorze mille six cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 Pour les descendants d’Issachar, classés par origine, familles, maisons paternelles: d’après le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 les recensés, dans la tribu d’lssachar, se montèrent à cinquante-quatre mille quatre cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 Pour les descendants de Zabulon, classés par origine, familles, maisons paternelles: suivant le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 les recensés, dans la tribu de Zabulon, se montèrent à cinquante-sept mille quatre cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 Quant aux tribus issues de Joseph: pour les descendants d’Ephraïm, classés selon leur origine, leurs familles, leurs maisons paternelles: suivant le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 les recensés, dans la tribu d’Ephraïm, se montèrent à quarante mille cinq cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 Pour les descendants de Manassé, classés selon leur origine, leurs familles, leurs maisons paternelles: d’après le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 les recensés, dans la tribu de Manassé, se montèrent à trente-deux mille deux cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 Pour les descendants de Benjamin, classés par origine, familles, maisons paternelles: suivant le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 les recensés, dans la tribu de Benjamin, se montèrent à trente-cinq mille quatre cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 Pour les descendants de Dan, classés par origine, familles, maisons paternelles: suivant le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 les recensés, dans la tribu de Dan, se montèrent à soixante-deux mille sept cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 Pour les descendants d’Asher, classés par origine, familles, maisons paternelles: suivant le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 les recensés, dans la tribu d’Asher, se montèrent à quarante et un mille cinq cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 Les descendants de Nephtali étant classés selon leur origine, leurs familles, leurs maisons paternelles: d’après le compte nominal de tous les hommes âgés de vingt ans et plus, aptes au service,
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 les recensés, dans la tribu de Nephtali, se montèrent à cinquante-trois mille quatre cents.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 Tel fut le dénombrement opéré par Moïse et Aaron conjointement avec les phylarques d’Israël, lesquels étaient douze, un homme par famille paternelle.
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 Le total des Israélites recensés selon leurs maisons paternelles, de tous ceux qui, âgés de vingt ans et au-delà, étaient propres au service en Israël,
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 le total de ces recensés fut de six cent trois mille cinq cent cinquante.
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 Quant aux Lévites, eu égard à leur tribu paternelle, ils ne figurèrent point dans ce dénombrement.
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 Et l’Éternel parla ainsi à Moïse:
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 "Pour ce qui est de la tribu de Lévi, tu ne la recenseras ni n’en feras le relevé en la comptant avec les autres enfants d’Israël.
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 Mais tu préposeras les Lévites au tabernacle du statut, à tout son attirail et à tout ce qui le concerne: ce sont eux qui porteront le tabernacle et tout son attirail, eux qui en feront le service, et qui doivent camper à l’entour.
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 Quand le tabernacle devra partir, ce sont les Lévites qui le démonteront, et quand il devra s’arrêter, ce sont eux qui le dresseront; le profane qui en approcherait serait frappé de mort.
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 Les enfants d’Israël se fixeront chacun dans son camp et chacun sous sa bannière, selon leurs légions;
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 et les Lévites camperont autour du tabernacle du statut, afin que la colère divine ne sévisse point sur la communauté des enfants d’Israël; et les Lévites auront sous leur garde le tabernacle du statut."
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 Les Israélites obéirent: tout ce que l’Éternel avait ordonné à Moïse, ils s’y conformèrent.
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.