< Néhémie 7 >

1 Lorsque le mur eut été reconstruit et que j’en eus posé les portes, les portiers, les chantres et les Lévites furent installés à leur poste.
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 Je confiai la garde de Jérusalem à mon frère Hanani et à Hanania, gouverneur du fort, car celui-ci passait pour un homme loyal et craignant Dieu comme peu de gens.
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 Je leur dis: "Les portes de Jérusalem ne devront pas s’ouvrir avant que le soleil chauffe; et pendant que les gardes seront encore là, qu’on ferme les battants et qu’on les verrouille. Qu’ensuite on pose les gardes des habitants de Jérusalem, chacun à son poste et chacun vis-à-vis de sa maison."
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 Or, la ville avait une grande étendue, et la population y était peu nombreuse, et toutes les maisons n’étaient pas rebâties.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 Dieu m’inspira la pensée de rassembler les nobles, les chefs et le peuple pour établir leur filiation; je découvris le registre généalogique de ceux qui étaient montés en premier, et j’y trouvai consigné ce qui suit:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 "Voici les gens de la province, parmi les captifs exilés que Nabuchodonosor, roi de Babylone, avait déportés à Babylone, qui partirent pour retourner à Jérusalem et en Judée, chacun dans sa ville.
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 Ils revinrent avec Zorobabel, Yêchoua, Nehémia, Azaria, Raamia, Nahamani, Mardochée, Bilchân, Mispéret, Bigvaï, Nehoum et Baana. Ainsi se chiffraient les hommes du peuple d’Israël:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 Les enfants de Paroch: deux mille cent soixante-douze;
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 les enfants de Chefatia: trois cent soixante-douze;
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 les enfants d’Arah: six cent cinquante-deux;
Zidzukulu za Ara 652
11 les enfants de Pahat-Moab, de la famille de Yêchoua et Joab: deux mille huit cent dix-huit;
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 les enfants d’Elam: mille deux cent cinquante-quatre;
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 les enfants de Zattou: huit cent quarante-cinq;
Zidzukulu za Zatu 845
14 les enfants de Zaccaï: sept cent soixante;
Zidzukulu za Zakai 760
15 les enfants de Binnouï: six cent quarante-huit;
Zidzukulu za Binuyi 648
16 les enfants de Bêbaï: six cent vingt-huit;
Zidzukulu za Bebai 628
17 les enfants d’Azgad: deux mille trois cent vingt-deux;
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 les enfants d’Ado-nikâm: six cent soixante-sept;
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 les enfants de Bigvaï: deux mille soixante-sept;
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 les enfants d’Adin: six cent cinquante-cinq;
Zidzukulu za Adini 655
21 les enfants d’Atêr de la famille de Yehiskia: quatre-vingt-dix-huit;
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 les enfants de Hachoum: trois cent vingt-huit;
Zidzukulu za Hasumu 328
23 les enfants de Bêçai: trois cent vingt-quatre;
Zidzukulu za Bezayi 324
24 les enfants de Harif: cent douze;
Zidzukulu za Harifu 112
25 les enfants de Gabaon quatre-vingt-quinze;
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 les gens de Bethléem et de Netofa: cent quatre-vingt-huit;
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 les gens d’Anatot: cent vingt-huit
Anthu a ku Anatoti 128
28 les gens de Beth-Azmaveth: quarante-deux;
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 les gens de Kiriath-Yearim, Kefira et Beêrot: sept cent quarante-trois;
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 les gens de Rama et Ghéba: six cent vingt-et-un;
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 les gens de Mikhmas: cent vingt-deux;
Anthu a ku Mikimasi 122
32 les gens de Béthel et Aï: cent vingt-trois;
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 les gens d’un autre Nebo: cinquante-deux;
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 les enfants d’un autre Elam: mille deux cent cinquante-quatre;
Ana a Elamu wina 1,254
35 les enfants de Harîm: trois cent vingt;
Zidzukulu za Harimu 320
36 les enfants de Jéricho: trois cent quarante-cinq;
Zidzukulu za Yeriko 345
37 les enfants de Lod, Hadid et Ono: sept cent vingt et un;
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 les enfants de Senaa: trois mille neuf cent trente.
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 Les prêtres: les fils de Yedaïa, de la famille de Yêchoua: neuf cent soixante-treize;
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 les enfants d’Immêr: mille cinquante-deux;
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 les enfants de Pachhour: mille deux cent quarante-sept;
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 les enfants de Harîm: mille dix-sept.
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 Les Lévites: les enfants de Yêchoua et Kadmiêl, descendants de Hodeva: soixante-quatorze.
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 Les chantres: les fils d’Assaph: cent quarante-huit.
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 Les portiers: les enfants de Challoum, les enfants d’Atêr, les enfants de Talmôn, les enfants d’Akkoub, les enfants de Hatita, les enfants de Chobaï: cent trente-huit.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 Les serviteurs du temple: les enfants de Ciha, les enfants de Hassoufa, les enfants de Tabbaot,
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 les enfants de Kêros, les enfants de Sis, les enfants de Padôn,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 les enfants de Lebana, les enfants de Hagaba, les enfants de Salmaï,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 les enfants de Hanân, les enfants de Ghiddêl, les enfants de Gahar,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 les enfants de Reaïa, les enfants de Recin, les enfants de Nekoda,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 les enfants de Gazzâm, les enfants d’Ouzza, les enfants de Passêah,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 les enfants de Bessaï, les enfants de Meounîm, les enfants de Nefichsîm,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 les enfants de Bakbouk, les enfants de Hakoufa, les enfants de Harhour,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 les enfants de Baçlit, les enfants de Mehida, les enfants de Harcha,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 les enfants de Barkôs, les enfants de Sissera, les enfants de Témah,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 les enfants de Neciah, les enfants de Hatifa.
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 Les descendants des esclaves de Salomon: les enfants de Sotaï, les enfants de Soféret, les enfants de Perida;
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 les enfants de Yaala, les enfants de Darkôn, les enfants de Ghiddêl;
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 les enfants de Chefatia, les enfants de Hattil, les enfants de Pokhéret-Hacebaïm, les enfants d’Amôn.
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 Tous les serviteurs du temple et les descendants des esclaves de Salomon s’élevaient au nombre de trois cent quatre-vingt-douze.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 Et voici ceux qui partirent de Têl-Mélah, de Têl-Harcha, Keroub, Addôn, Immêr, et qui ne purent indiquer leur famille et leur filiation pour établir qu’ils faisaient partie d’Israël:
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 les enfants de Delaïa, les enfants de Tobia, les enfants de Nekoda, au nombre de six cent quarante-deux.
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 Et parmi les prêtres: les enfants de Hobaïa, les enfants de Hakoç, les enfants de Barzillaï, qui avait pris pour femme une des filles de Barzillaï, le Galaadite, et en avait adopté le nom.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 Ceux-là recherchèrent leurs tables de généalogie, mais elles ne purent être retrouvées; aussi furent-ils déchus du sacerdoce.
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 Le gouverneur leur défendit de manger des choses éminemment saintes, jusqu’au jour où officierait de nouveau un prêtre portant les Ourîm et les Toumîm.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 Toute la communauté réunie comptait quarante-deux mille trois cent soixante individus,
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 sans compter leurs esclaves et leurs servantes, au nombre de sept mille trois cent trente-sept, auxquels s’ajoutaient des chanteurs et des chanteuses, au nombre de deux cent quarante-cinq.
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 quatre cent trente-cinq chameaux, six mille sept cent vingt ânes.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 Une partie des chefs de famille firent des dons pour les travaux; le gouverneur versa au trésor mille dariques d’or, cinquante bassins, cinq cent trente tuniques de prêtres.
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 Un certain nombre de chefs de famille donnèrent au trésor des travaux: en or, vingt mille dariques, et en argent, deux mille deux cents mines.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 Et ce que donna le reste du peuple s’éleva, en or, à vingt mille dariques, en argent, à deux mille mines, et, en tuniques de prêtres, à soixante-sept.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 Les prêtres, les Lévites, les portiers, les chanteurs, une partie du peuple, les serviteurs du temple et tout Israël s’établirent dans leurs villes respectives. Lorsque le septième mois arriva, les enfants d’Israël étaient installés dans leurs villes."
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

< Néhémie 7 >