< Nahum 2 >

1 Le destructeur s’avance contre toi: veille sur la forteresse, observe la route, affermis tes reins, ramasse toutes tes forces!
Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
2 Car le Seigneur rétablit la grandeur de Jacob comme la grandeur d’Israël, puisque des pillards les avaient dépouillés, et avaient ruiné leurs sarments.
Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
3 Les boucliers de ses héros sont teints de rouge, ses hommes de guerre sont vêtus de pourpre. Ses chars jettent des éclats de flamme au jour où il les met en ligne, et les lances sont mises en mouvement.
Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
4 Les chars tourbillonnent dans les rues, bondissent à travers les places; à les voir, on dirait des torches, ils se précipitent comme des éclairs.
Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
5 Il s’en rapporte à ses braves: ils trébuchent dans leur marche, se hâtent vers les remparts de la ville, et on prépare l’abri couvert.
Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
6 Les portes protégées par les cours d’eau sont enfoncées et le palais en est atterré.
Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
7 Houzab la reine est tirée de sa cachette et emmenée, tandis que ses servantes poussent des soupirs, telles des colombes qui gémissent, et se frappent la poitrine.
Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
8 Or, Ninive était de tout temps comme un réservoir plein d’eau; et maintenant ils fuient! "Arrêtez! Tenez bon!" Mais personne ne se retourne.
Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
9 Pillez de l’or! Pillez de l’argent! Infinis sont les trésors: c’est toute une richesse de vases précieux!
Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 Tout est pillé, dépouillé, ravagé! Les cœurs se sentent défaillir, les genoux vacillent, tous les reins sont saisis de tremblement, tous les visages se couvrent de pâleur.
Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
11 Qu’est-il advenu de ce repaire de lions, où se gorgeaient les lionceaux, où se rencontraient lion, lionne et lionceau, que personne n’osait troubler?
Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Le lion déchirait la proie pour ses petits, il l’étranglait pour ses lionnes; il remplissait ses antres de victuailles et ses tanières de bêtes mises en pièces.
Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13 Voici, je m’apprête contre toi, dit l’Eternel-Cebaot: je brûlerai tes chars dans un nuage de fumée; tes lionceaux, le glaive les dévorera. Je mettrai fin à tes rapines sur la terre, et l’on n’entendra plus la voix de tes hérauts.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”

< Nahum 2 >