< Josué 24 >

1 Josué réunit toutes les tribus d’Israël à Sichem; puis il appela les anciens d’Israël, ses chefs, ses juges et ses préposés, qui se placèrent en présence de Dieu.
Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
2 Et Josué dit à tout le peuple: "Ainsi a parlé l’Eternel, Dieu d’Israël: "Vos ancêtres habitaient jadis au-delà du Fleuve, jusqu’à Tharé, père d’Abraham et de Nahor, et ils servaient des dieux étrangers.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
3 Je pris votre père, Abraham, des bords du Fleuve, le fis voyager par tout le pays de Canaan, lui donnai une nombreuse postérité, et le rendis père d’Isaac.
Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
4 A Isaac je donnai Jacob et Esaü; j’attribuai à Esaü la montagne de Séïr pour sa possession, Jacob et ses enfants descendirent en Egypte.
ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
5 Je suscitai Moïse et Aaron, j’accablai l’Egypte par tout ce que je fis au milieu d’elle, après quoi je vous en fis sortir.
“‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
6 Quand j’eu fait sortir vos pères de l’Egypte et que vous fûtes parvenus jusqu’à la mer, les Egyptiens poursuivirent vos pères, avec chars et cavaliers, vers la mer des Joncs.
Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
7 Ceux-ci implorèrent l’Eternel, qui interposa un épais nuage entre vous et les Egyptiens, fit retomber sur eux la mer et les submergea vous avez vu de vos yeux ce que j’ai fait à l’Egypte puis vous demeurâtes de longs jours au désert.
Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
8 Je vous conduisis au pays des Amorréens, établis au bord du Jourdain, et qui vous combattirent; je les livrai en votre pouvoir, vous conquîtes leur pays, et je les exterminai devant vous.
“‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
9 Puis se leva Balak, fis de Cippor, roi de Moab, qui entra en lutte avec Israël, et fit appeler Balaam, fils de Beor, pour vous maudire.
Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
10 Mais je ne voulus pas écouter Balaam, et il dut au contraire vous bénir, et je vous sauvai ainsi de sa main.
Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
11 Puis vous traversâtes le Jourdain et arrivâtes devant Jéricho; et vous eûtes contre vous les possesseurs de Jéricho, les Amorréens, les Phérézéens, les Cananéens, les Héthéens, le Ghirgachéens, les Hévéens et les Jébuséens; mais je les livrai en votre pouvoir.
“‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
12 Je vous ai aussi fait précéder par les frelons, qui ont chassé de devant vous les deux rois des Amorréens, ce que tu ne dois ni à ton épée ni à ton arc.
Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
13 Je vous ai ainsi donné un pays qui ne vous a coûté aucune peine; des villes où vous vous êtes installés sans les avoir bâties, des vignes et des oliviers dont vous jouissez sans les avoir plantés."
Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
14 A votre tour, révérez et servez l’Eternel avec droiture, avec sincérité; repoussez les dieux que vos pères ont adorés au-delà du Fleuve et en Egypte, et n’adorez que l’Eternel.
“Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
15 Que s’il vous déplaît de servir l’Eternel, choisissez dès à présent qui vous voulez servir, soit les dieux qu’adoraient vos pères au-delà du Fleuve, soit les dieux des Amorréens dont vous occupez le pays: pour moi et ma famille, c’est l’Eternel que nous servons!"
Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
16 Le peuple répondit: "Loin de nous la pensée de renoncer à l’Eternel pour servir des dieux étrangers!
Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
17 C’Est l’Eternel qui est notre Dieu, c’est lui qui nous a fait monter nous et nos pères, du pays d’Egypte, cette maison d’esclaves; qui a fait à nos yeux tant de grands miracles, qui nous a protégés constamment dans notre voie, parmi tous les peuples au milieu desquels nous avons passé.
Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
18 C’Est l’Eternel qui a repoussé devant nous l’Amorréen et les autres peuples habitant la contrée: nous aussi nous entendons servir l’Eternel, car c’est lui notre Dieu."
Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
19 Et Josué dit au peuple: "Vous ne pourrez pas aisément servir l’Eternel; car c’est un Dieu saint, un Dieu jaloux, qui ne supporterait ni vos offenses ni vos péchés.
Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
20 Si vous abandonnez l’Eternel pour servir les dieux de l’étranger, à son tour il vous maltraitera et consommera votre ruine, après avoir été votre bienfaiteur."
Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
21 Et le peuple répondit à Josué: "Non, nous voulons servir l’Eternel."
Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
22 Alors Josué dit au peuple: "Vous êtes témoins contre vous-mêmes, que c’est pour le culte de l’Eternel que vous avez opté!" Ils répondirent: "Nous le sommes."
Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
23 "Eh bien! Répudiez donc les dieux de l’étranger qui sont au milieu de vous, et tournez uniquement vos coeurs vers l’Eternel, Dieu d’Israël."
Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
24 Et le peuple dit à Josué: "C’Est l’Eternel, notre Dieu, que nous servirons, c’est à sa voix que nous voulons obéir."
Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
25 En ce jour même, Josué établit un pacte avec le peuple, et lui imposa une loi et des statuts à Sichem.
Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
26 Puis Josué consigna ces choses dans le livre de la loi divine; il prit aussi une grande pierre qu’il dressa en ce lieu, sous le chêne qui était dans le lieu consacré à l’Eternel.
Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
27 Et Josué dit à tout le peuple: "Cette pierre nous servira de témoin, car elle a entendu toutes les paroles que l’Eternel nous a adressées; elle serait un témoin contre vous, si vous veniez à renier votre Dieu."
Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
28 Et Josué congédia le peuple, chacun rentrant dans son territoire.
Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
29 Après ces événements, Josué, fils de Noun, serviteur de l’Eternel, mourut âgé de cent dix ans.
Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
30 On l’ensevelit dans les limites de sa possession, à Timnath-Sérah, dans la montagne d’Ephraïm, au nord du mont Gaach.
ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
31 Israël resta attaché au Seigneur tant que vécut Josué, et tout le temps que continuèrent à vivre, après lui, les vieillards témoins de tout ce que le Seigneur avait fait pour Israël.
Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
32 Quant aux ossements de Joseph, que les enfants d’Israël avaient emportés d’Egypte, on les inhuma à Sichem, dans la pièce de terre que Jacob avait acquise, pour cent kecita, des fils de Hamor, père de Sichem, et qui devint la propriété des enfants de Joseph.
Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
33 Eléazar, fils d’Aaron, étant mort, on l’ensevelit sur la colline de Phinéas, son fils, qu’on lui avait donnée dans la montagne d’Ephraïm.
Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.

< Josué 24 >