< Josué 14 >

1 Voici maintenant les possessions des Israélites dans le pays de Canaan, qui leur furent réparties par le prêtre Eléazar et Josué, fils de Noun, assistés des chefs de famille des tribus d’Israël.
Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
2 Cette répartition se fit au sort, comme l’Eternel l’avait ordonné par Moïse, entre les neuf tribus et demie.
Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
3 Car Moïse avait assigné leur patrimoine aux deux autres tribus et demie au delà du Jourdain, mais n’avait pas assigné de terre patrimoniale aux Lévites,
Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
4 d’autant que les fils de Joseph formèrent deux tribus, Manassé et Ephraïm; on ne donna donc point de part aux Lévites dans le pays, si ce n’est certaines villes pour y demeurer, avec les banlieues pour leurs bestiaux et autres biens qu’ils possédaient.
Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
5 Les Israélites procédèrent, dans le partage du pays, selon ce que l’Eternel avait ordonné à Moïse.
Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 Les enfants de Juda s’étaient présentés devant Josué à Ghilgal, et Caleb, fils de Yefounné, le Kenizzéen, lui avait dit: "Tu sais ce que l’Eternel a dit à Moïse, l’homme de Dieu, sur mon compte et sur le tien, à Kadêch-Barnéa.
Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
7 J’Étais âgé de quarante ans, lorsque Moïse, serviteur de l’Eternel, m’envoya de Kadêch-Barnéa pour explorer ce pays, et je lui en fis un rapport conforme à ma pensée.
Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
8 Mes frères, qui y étaient allés avec moi, jetèrent le découragement parmi le peuple, mais moi je restai fidèle à l’Eternel, mon Dieu.
Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
9 Ce jour-là, Moïse me fit un serment, en disant: "Assurément, ce pays qu’a foulé ton pied t’appartiendra, comme un patrimoine, à toi et à tes descendants pour toujours, parce que tu es resté fidèle à l’Eternel, mon Dieu.
Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
10 Effectivement, l’Eternel m’a conservé la vie, comme il l’avait annoncé. Voici quarante-cinq ans que l’Eternel adressa cette parole à Moïse, alors qu’Israël voyageait dans le désert, et voici qu’à présent j’ai quatre-vingt-cinq ans.
“Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
11 Robuste encore comme le jour où Moïse me donna cette mission, j’ai la même vigueur aujourd’hui qu’alors, pour la guerre et pour toute expédition.
Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
12 Donne-moi donc cette montagne, que l’Eternel me promit ce jour-là: tu as appris à cette époque que des Anakéens y habitaient, que les villes y sont grandes et fortes; si l’Eternel m’assiste, je les déposséderai, comme l’Eternel l’a dit."
Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
13 Josué bénit Caleb, fils de Yefounné, et lui donna Hébron comme héritage.
Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
14 C’Est pourquoi, Hébron est resté, jusqu’à ce jour, le partage de Caleb, fils de Yefounné, le Kenizzéen, en récompense de sa fidélité à l’Eternel, Dieu d’Israël.
Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
15 Or, le nom primitif de Hébron était: la Cité d’Arba, qui était le plus grand des Anakéens. Et le pays, délivré de la guerre, demeura tranquille.
(Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.

< Josué 14 >