< Job 41 >

1 Tireras-tu le Léviathan avec un hameçon? Lui feras-tu baisser la langue avec la ligne?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Lui passeras-tu un jonc dans les narines, lui perceras-tu la mâchoire avec un crochet?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Te prodiguera-t-il ses prières? Ou t’adressera-t-il de douces paroles?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Fera-t-il un pacte avec toi? L’Engageras-tu comme un esclave perpétuel?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Te servira-t-il de jouet comme un passereau? L’Attacheras-tu pour amuser tes jeunes filles?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Les pêcheurs associés en feront-ils le commerce? Le débiteront-ils entre les marchands?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Cribleras-tu sa peau de dards et sa tête de harpons barbelés?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Pose seulement ta main sur lui: tu te souviendras de ce combat et ne recommenceras plus!
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Vois, espérer la victoire est une illusion: à son seul aspect, n’est-on pas terrassé?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Personne n’est assez téméraire pour l’exciter: qui donc oserait me tenir tête, à moi?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Qui m’a rendu un service que j’aie à payer de retour? Tout ce qui est sous le ciel est à moi.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Je ne passerai pas sous silence ses membres, le détail de ses exploits, la beauté de sa structure.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Qui a soulevé le dessous de son vêtement? Qui a pénétré dans la double rangée de sa denture?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Qui a ouvert les battants de sa gueule? La terreur habite autour de ses dents.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Imposantes sont les lignes d’écailles qui lui servent de boucliers et pressées comme un sceau qui adhère fortement.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Elles se touchent de près, l’air ne pénètre pas entre elles.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 L’Une est serrée contre l’autre; elles tiennent ensemble sans aucun interstice.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Ses éternuements font jaillir la lumière, ses yeux sont comme les paupières de l’aurore.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 De sa bouche partent des flammes, s’échappent des étincelles de feu.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 De ses naseaux sort la fumée, comme d’une marmite bouillante chauffée aux roseaux.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Son haleine allume les charbons, de sa gueule sort une flamme.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 Dans son cou la force réside, devant lui bondit la terreur.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Les fanons de sa chair sont adhérents, soudés sur lui sans ballotter.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Son cœur est massif comme une pierre, solide comme la meule de dessous.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Quand il se dresse, les plus vaillants tremblent et se dérobent sous le coup de l’épouvante.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 L’Attaque-t-on avec l’épée, elle n’a point de prise sur lui, pas plus que lance, javelot ou cuirasse.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Pour lui, le fer est comme de la paille, l’airain comme du bois pourri.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Le fils de l’arc ne le met pas en fuite, les pierres de la fronde se changent pour lui en chaume.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Comme du chaume aussi lui paraît la massue, il se rit du sifflement des dards.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Son ventre est garni de tessons pointus, il promène comme une herse sur le limon.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Il fait bouillonner les profondeurs comme une chaudière; il rend la mer semblable à un bassin d’onguents.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Le sillage qu’il laisse derrière lui est lumineux: on dirait que les vagues ont la blancheur de la vieillesse.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Il n’a pas son pareil sur la terre, lui qui est fait pour ne rien craindre.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Il regarde avec dédain tout ce qui est élevé: il est le roi de tous les fauves altiers.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< Job 41 >