< Job 36 >
1 Elihou, poursuivant, dit:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Accorde-moi un peu d’attention, et je t’instruirai; car il reste encore des arguments en faveur de Dieu.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Je tirerai ma science de loin, et j’établirai l’équité de mon Dieu.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Car certes, mes paroles ne sont pas mensongères: c’est quelqu’un aux connaissances sûres qui est devant toi.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Vois, Dieu est puissant et il ignore le dédain; il est souverain par la force de la raison.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Il ne laisse point vivre le méchant, mais il fait triompher le bon droit des pauvres.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Il ne détourne pas les yeux des justes, qu’il met de pair avec les rois sur le trône: il les installe solidement et les fait grandir.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 Que s’ils sont enchaînés dans les fers, pris dans les liens de la misère,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 et qu’après leur avoir représenté leurs actes et leurs péchés, fruits de l’orgueil,
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 il ouvre leur oreille à la réprimande et les exhorte à revenir de l’iniquité,
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 s’ils écoutent et se soumettent, ils achèveront leurs jours dans le bonheur et leurs années dans les délices.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Mais s’ils n’écoutent point, ils finiront pas l’épée et périront faute d’intelligence.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Pervers de cœur, ils manifestent de la colère, refusent d’implorer Dieu quand il les charge de chaînes.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Aussi leur âme périt-elle en pleine jeunesse, leur vie s’éteint comme celle des infâmes libertins.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Mais le malheureux, il le sauve par sa misère même, et par la souffrance il ouvre son oreille aux conseils.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Aussi bien, il te fera passer de l’étreinte de l’adversité en un lieu spacieux, où n’existe nulle gène, et ta table sera couverte de mets succulents.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Si tu as subi pleinement le châtiment du méchant, c’est que châtiment et justice sont une force.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Crains donc que le dépit ne t’attire de nouveaux coups; ne te laisse pas égarer par la grandeur de la rançon.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Dieu peut-il priser assez tes cris suppliants pour t’épargner souffrances et durs efforts?
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 N’Aspire point à la nuit, où les peuples sont enlevés de leur place.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Garde-toi de te laisser aller au mal, car tu sembles le préférer à la souffrance.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Vois, Dieu est sublime dans sa force: existe-t-il un guide comme lui?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Qui lui dicte la voie qu’il doit suivre? Qui lui dira: "Tu commets des injustices?"
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Prends à cœur d’exalter son œuvre, que les humains célèbrent par leurs chants.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Les hommes l’admirent, le mortel la contemple de loin.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Oui, Dieu est grand: nous ne pouvons le comprendre; le nombre de ses années est incalculable.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 Il attire les gouttes d’eau qui, à la suite de son brouillard, se résolvent en pluie.
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Les nuages en ruissellent et s’épandent sur la foule des humains.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Sait-on seulement comprendre le déploiement des nuées, le fracas de son pavillon?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Vois, il s’enveloppe de sa lumière et il en couvre les profondeurs de cet océan de nuages.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Car il se sert d’eux pour juger les peuples ou leur donner de la nourriture en abondance.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Il recouvre ses mains de flammes, qu’il dirige contre les rebelles.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Il révèle sa présence par son tonnerre, Instrument de colère contre les présomptueux.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.