< Job 29 >

1 Job, poursuivant l’exposé de son thème, dit:
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Ah! Que ne suis-je tel que j’étais aux temps passés, aux jours où Dieu me protégeait;
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 où son flambeau brillait sur ma tête, et où sa lumière me guidait dans les ténèbres;
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 tel que j’étais aux jours de mon automne, alors que l’amitié de Dieu s’étendait sur ma demeure;
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 que le Tout-Puissant était encore avec moi et que j’étais entouré de mes jeunes gens;
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 quand je baignais mes pieds dans la crème, et que le rocher ruisselait pour moi de flots d’huile!
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 Quand je me dirigeais vers la Porte, au seuil de la cité, et fixais mon siège sur la place publique,
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 les jeunes, en me voyant, se cachaient; les vieillards se levaient et se tenaient debout.
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 Les grands retenaient leurs paroles et posaient la main sur la bouche.
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 La voix des seigneurs expirait sur leurs lèvres, et leur langue se collait à leur palais;
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 car l’oreille qui m’entendait me proclamait heureux, et l’œil qui me voyait rendait témoignage pour moi.
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 C’Est que je sauvais le pauvre, criant au secours, et l’orphelin sans soutien.
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 La bénédiction du désespéré allait à moi, et je mettais de la joie au cœur de la veuve.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 Je me revêtais d’équité comme d’une parure, mon esprit de justice était mon manteau et mon turban.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 J’Étais les yeux de l’aveugle, j’étais les pieds du boiteux.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 J’Étais un père pour les malheureux; la cause de l’inconnu, je l’étudiais à fond.
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 Je brisais la mâchoire du malfaiteur, et j’arrachais la proie d’entre ses dents.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 Et je disais: "Je finirai avec mon nid; comme le phénix je vivrai de longs jours.
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 Ma racine sera en contact avec l’eau, la rosée se posera, la nuit, sur mon branchage.
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 Ma gloire se renouvellera sans cesse, et mon arc se rajeunira dans ma main."
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 Ils m’écoutaient, pleins d’attente; ils faisaient silence pour entendre mon avis.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 Quand j’avais fini de parler, ils ne répliquaient pas, et mes discours s’épandaient sur eux.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 Ils m’attendaient comme la pluie; ils ouvraient la bouche comme pour l’ondée printanière.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 Je leur souriais et ils n’osaient y croire; jamais ils n’éteignaient le rayonnement de ma face.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 Volontiers j’allais vers eux, m’asseyant à leur tête, et j’étais comme un roi dans son armée, comme quelqu’un: qui console des affligés.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

< Job 29 >