< Job 28 >

1 Certes, il existe des mines pour l’argent et des gîtes pour 'l’or que l’on affine.
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Le fer est extrait du sol, et la roche, fondue, donne du cuivre.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 Le mineur a posé des limites à l’obscurité; jusqu’aux extrêmes profondeurs il va chercher le minerai caché dans les ténèbres et l’ombre de la mort.
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 Il perce des tranchées à l’écart des habitations; ignoré du pied des passants, il est suspendu et ballotté loin des hommes.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 La terre d’où sort le pain, ses entrailles sont bouleversées comme par le feu.
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 Ses pierres sont des nids de saphirs, et là s’offre au regard la poudre d’or.
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 On y arrive par un chemin que l’oiseau de proie ne connaît pas, que l’œil du vautour ne distingue point.
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 Les fauves altiers ne l’ont pas foulé, le lion ne l’a pas franchi.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 Le mineur porte la main sur le granit, et il remue les montagnes jusqu’à leur racine.
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 Il perce des galeries à travers les roches, et son œil contemple les plus rares richesses.
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 Il aveugle les voies d’eau pour empêcher Ies infiltrations et amène au jour ce qui était caché.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 Mais la Sagesse, où la trouver? Où est le siège de la Raison?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Le mortel n’en connaît pas le prix, elle est introuvable au pays des vivants.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 L’Abîme dit: "Elle n’est pas dans mon sein!" Et la mer dit: "Elle n’est pas chez moi!"
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 On ne peut l’acquérir pour de l’or de choix, on ne l’achète pas au poids de l’argent.
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 L’Or d’Ophir ne correspond pas à sa valeur, ni l’onyx précieux, ni le saphir.
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Ni or ni verre ne peuvent rivaliser avec elle; aucun vase d’or fin ne paie son prix.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 Ni corail ni cristal n’entrent en compte; la possession de la sagesse vaut mieux que les perles.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 La topaze d’Ethiopie ne l’égale point; on ne peut la mettre en balance avec l’or pur.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 Oui, la Sagesse d’où vient-elle? Où est le siège de la Raison?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Elle se dérobe aux yeux de tout vivant, elle est inconnue à l’oiseau du ciel.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 L’Abîme et la mort disent: "De nos oreilles nous avons entendu parler d’elle."
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 C’Est Dieu qui en sait le chemin, c’est lui qui en connaît le siège.
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 Car ses regards portent jusqu’aux confins de la terre; tout ce qui est sous les cieux, il le voit.
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Lorsqu’il donna au vent son équilibre et détermina la mesure des eaux,
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 lorsqu’il traça sa loi à la pluie et sa voie à l’éclair sonore,
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 c’est alors qu’il l’a vue et appréciée à sa valeur, c’est alors qu’il en a marqué la place et pénétré le fond,
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 et il a dit à l’homme: "Ah! La crainte du Seigneur, voilà la Sagesse; éviter le mal, voilà la Raison."
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”

< Job 28 >