< Job 17 >

1 Mon âme est meurtrie, mes jours s’éteignent, la tombe m’attend.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Ne suis-je pas en butte à des moqueries? Mes yeux ne sont-ils pas constamment témoins de leurs perfidies?
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Ah! De grâce, accorde-moi ta caution! Sois toi-même mon garant vis-à-vis de toi qui voudrait s’engager pour moi?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 Car tu as fermé leur cœur à la raison; aussi ne les laisseras-tu pas triompher.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 Pour une part de butin on trahit des amis, de sorte que les yeux de leurs enfants se consument de misère.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 On a fait de moi la fable des nations; je suis l’homme à qui on crache au visage.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 Mes yeux sont éteints par le chagrin, et tous mes organes sont comme une ombre.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Les gens de bien en sont stupéfaits, et l’innocent en est révolté contre l’impie.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 Cependant le juste persiste dans sa conduite, et celui qui a les mains pures redouble d’énergie.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 Quant à vous, retournez-vous donc tous contre moi, venez! Je ne trouverai pas un sage parmi vous.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Mes jours ont fui, mes projets sont ruinés, ces trésors de mon cœur.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 De la nuit ils veulent faire le jour, ils disent la lumière plus proche que les ténèbres.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Si je n’attends plus d’autre demeure que le Cheol, si j’ai étendu ma couche dans la région des ombres; (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 si je dis au tombeau: "Tu es mon père!" et à la vermine: "Tu es ma mère et ma sœur"
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 où donc est mon espérance? Mon espérance, qui peut la voir?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 Elle a sombré jusqu’au fond du Cheol, si toutefois le repos est assuré dans la poussière. (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Job 17 >