< Job 11 >

1 Çophar de Naama prit la parole et dit:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2 Est-ce que ce flot de paroles n’appelle pas une réponse? Suffit-il d’être loquace pour avoir raison?
“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
3 Ton verbiage réduirait-il les gens au silence, et prodiguerais-tu l’ironie, sans que personne te confonde?
Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
4 Tu dis: "Pure est ma doctrine, je suis sans tache à tes yeux."
Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
5 Ah! Il serait à souhaiter que Dieu parlât, qu’il ouvrît ses lèvres pour te répondre!
Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
6 Il te révélerait les mystères de la sagesse, car la vérité a de nombreux aspects; et tu reconnaîtrais que Dieu est loin de te compter toutes tes fautes.
ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
7 Prétends-tu pénétrer le secret insondable de Dieu, saisir la perfection du Tout-Puissant?
“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
8 Si elle a la hauteur des cieux, que peux-tu faire? Si elle dépasse la profondeur du Cheol, quelle connaissance en as-tu? (Sheol h7585)
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
9 Elle est plus étendue en longueur que la terre, plus vaste que l’Océan!
Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
10 Si Dieu s’avance, s’il enferme dans une geôle, s’il convoque une assemblée de justice, qui peut l’en détourner?
“Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
11 Car il connaît bien les gens pervers, il remarque l’iniquité sans même y regarder de près.
Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
12 Par là, l’homme au cerveau creux peut devenir intelligent et, cessant d’être un âne sauvage, naître à la dignité humaine.
Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
13 Donc, si tu veux, toi, bien diriger ton cœur et étendre tes bras vers lui,
“Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
14 si tu écartes le péché qui souille ta main, si tu bannis l’injustice de ta tente,
ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
15 aussitôt, tu pourras relever ton front exempt de tache; tu seras solide comma l’airain et n’auras rien à craindre.
udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
16 Bien plus, tu oublieras les maux passés, ou ne t’en souviendras que comme de l’onde écoulée.
Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
17 Ton sort sera plus brillant que le soleil de midi, le sombre crépuscule luira pour toi comme le matin.
Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
18 Tu seras plein de confiance, car l’espoir renaîtra, tu feras ton inspection et te coucheras en sécurité.
Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
19 Ton gîte ne sera troublé par personne, mais beaucoup rechercheront tes faveurs,
Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
20 tandis que les yeux des méchants se consumeront, que tout refuge leur sera fermé, et que leur espoir, ce sera le dernier souffle d’un mourant.
Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”

< Job 11 >