< Jérémie 50 >

1 Parole que prononça l’Eternel au sujet de Babel, du pays des Chaldéens par l’organe de Jérémie le prophète:
Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
2 "Annoncez-le parmi les nations, proclamez-le, dressez un signal, publiez-le sans rien dissimuler! dites: Babel est prise, Bel est confondu, Merodac est abattu; ses divinités sont couvertes de honte, ses idoles sont en pièces.
“Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina, kweza mbendera ndipo ulengeze; usabise kanthu, koma uwawuze kuti, ‘Babuloni wagwa; mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi, nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha. Milungu yake yagwidwa ndi mantha ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
3 Car du Nord un peuple s’avance contre elle, qui fait de son territoire une solitude où nul n’habite plus: hommes et bêtes, tous émigrent, s’en vont.
Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni ndi kusandutsa bwinja dziko lake. Kumeneko sikudzakhalanso munthu kapena nyama.
4 En ces jours et en ce temps-là, dit le Seigneur, les fils d’Israël unis aux fils de Juda reviendront; ils chemineront, tout en pleurant, à la recherche de l’Eternel, leur Dieu.
“Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
5 C’Est de Sion qu’ils s’enquerront, le visage tourné dans sa direction; ils viendront et s’attacheront au Seigneur par un pacte éternel, qui ne sera pas oublié.
Adzafunsa njira ya ku Ziyoni ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko. Iwo adzadzipereka kwa Yehova pochita naye pangano lamuyaya limene silidzayiwalika.
6 Mon peuple se composait de brebis égarées; leurs pasteurs les avaient fourvoyées, les laissant errer par les montagnes; elles vaguaient de hauteur en hauteur; oublieuses de leur gîte.
“Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika; abusa awo anawasocheretsa mʼmapiri. Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda mpaka kuyiwala kwawo.
7 Tous ceux qui les rencontraient en faisaient leur pâture, et leurs ennemis disaient: "Nous ne faisons pas de mal, puisqu’ils ont péché contre l’Eternel, leur abri véridique, contre l’Eternel, espoir de leurs ancêtres."
Aliyense amene anawapeza anawawononga; adani awo anati, ‘Ife si olakwa, chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
8 Fuyez de l’enceinte de Babel, sortez du pays des Chaldéens, et soyez comme des béliers à la tête du troupeau!
“Thawaniko ku Babuloni; chokani mʼdziko la Ababuloni. Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
9 Car voici, du pays du Nord je fais surgir et marcher sur Babel une ligue de grandes nations, qui feront campagne contre elle, et c’est ainsi qu’elle sera prise. Leurs flèches ressemblent à un guerrier triomphant qui ne subit pas d’échec.
Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto kudzamenyana ndi Babuloni. Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni. Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso, yosapita padera.
10 La Chaldée sera mise à sac; tous ceux qui la pilleront seront comblés, dit le Seigneur.
Motero Ababuloni adzafunkhidwa; ndipo onse omufunkha adzakhuta,” akutero Yehova.
11 Ah! réjouissez-vous, triomphez donc, vous les spoliateurs de mon héritage! Oui, ébattez-vous comme une génisse qui foule le blé et hennissez comme de fiers coursiers!
“Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika. Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala. Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
12 Elle va être entièrement confondue, votre mère; celle qui vous a donné le jour va connaître la rougeur de la honte. Tel sera le sort de ces nations: l’abandon, la ruine, la solitude.
Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri. Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa. Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse. Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
13 Par suite de la colère du Seigneur, elle deviendra inhabitable, complètement désolée. Quiconque passera près de Babel Sera stupéfait et ricanera à la vue de toutes ses plaies.
Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu ndipo adzakhala chipululu chokhachokha. Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
14 A vos rangs de bataille contre Babel, tout autour, vous tous qui bandez l’arc! tirez sur elle, ne ménagez pas les flèches, car elle s’est rendue coupable envers l’Eternel.
“Inu okoka uta, konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse. Muponyereni mivi yanu yonse chifukwa anachimwira Yehova.
15 Poussez le cri de guerre contre elle de toutes parts: elle tend les mains, ses créneaux tombent, ses murs s’écroulent, car ce sont les représailles de l’Eternel. Vengez-vous sur elle, faites-lui ce qu’elle a fait elle-même.
Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja. Nsanja zake zagwa. Malinga ake agwetsedwa. Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova. Mulipsireni, mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
16 Exterminez dans Babel quiconque sème et quiconque manie la faucille au temps de la moisson. Devant le glaive meurtrier, que chacun se dirige vers son peuple, que chacun se réfugie dans son pays!
Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense, ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola. Poona lupanga la ozunza anzawo, aliyense adzabwerera kwa anthu ake; adzathawira ku dziko la kwawo.
17 Israël était une brebis pourchassée, que des lions avaient mise en fuite; le roi d’Assyrie fut le premier à le dévorer et voilà que ce dernier lui a broyé les os, Nabuchodonosor, roi de Babylone.
“Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika pothamangitsidwa ndi mikango. Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo. Wotsiriza anali Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
18 Aussi l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël, s’exprime-t-il en ces termes: Je vais demander des comptes au roi de Babylone et à son pays comme j’ai demandé des comptes au roi d’Assyrie.
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
19 Et je ramènerai Israël à son pâturage, il pâturera sur le Carmel et le Basan, et sur le mont d’Ephraim et le Ghilead il se nourrira à satiété.
Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani; adzadya nakhuta ku mapiri a ku Efereimu ndi Giliyadi.
20 En ces jours et en ce temps-là, dit le Seigneur, on recherchera le péché d’Israël, et il aura disparu, les prévarications de Juda, et on ne les retrouvera point; car mon pardon est assuré à ceux que j’aurai conservés.
Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe, ndipo adzafufuza machimo a Yuda, koma sadzapeza ndi limodzi lomwe, chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
21 Sus au pays de "la double rébellion" et aux habitants de la ville du "châtiment!" Frappe par l’épée, extermine-les jusqu’au bout, dit le Seigneur, et exécute tout ce que je t’ai ordonné.
“Lithireni nkhondo dziko la Merataimu ndi anthu okhala ku Pekodi. Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,” akutero Yehova. “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
22 Un bruit de guerre retentit dans le pays, c’est une chute terrible.
Mʼdziko muli phokoso la nkhondo, phokoso la chiwonongeko chachikulu!
23 Comme il est abattu et brisé, le marteau qui broyait toute la terre! Comme elle est devenue, cette Babel, une ruine parmi toutes les nations!
Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi. Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ina!
24 Je t’ai dressé un piège, ô Babel, et tu y as été prise, sans t’en apercevoir; te voilà atteinte et appréhendée, parce que tu t’étais insurgée contre le Seigneur!
Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.
25 L’Eternel a ouvert son arsenal, et en a sorti les instruments de sa colère, car il y a une oeuvre à accomplir pour l’Eternel-Cebaot sur la terre des Chaldéens.
Yehova watsekula nyumba ya zida zake ndipo watulutsa zida za ukali wake, pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire mʼdziko la Ababuloni.
26 Marchez contre elle de toutes les extrémités, ouvrez ses greniers, piétinez-la comme des javelles, détruisez-la: que rien d’elle ne subsiste!
Mumenyane naye Babuloni mbali zonse. Anthu ake muwawunjike ngati milu ya tirigu. Muwawononge kotheratu ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
27 Frappez du glaive tous ses taureaux! Qu’ils s’en aillent à la boucherie! Malheur à eux, car leur jour est arrivé, le temps de leur châtiment!
Iphani ankhondo ake onse. Onse aphedwe ndithu. Tsoka lawagwera pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
28 Entendez les cris des fuyards, de ceux qui se sauvent du pays de Babei, annonçant dans Sion les représailles de l’Eternel, notre Dieu, la revanche de son sanctuaire.
Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni akulengeza mu Yerusalemu za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu. Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
29 Convoquez contre Babel des archers, tous les tireurs d’arbalète; cernez-la de toutes parts. Point de merci pour elle! Payez-la selon ses oeuvres, faites-lui comme elle a fait elle-même; car elle a défié le Seigneur, le Saint d’Israël.
“Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni. Muyitanenso onse amene amakoka mauta. Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira; musalole munthu aliyense kuthawa. Muchiteni monga momwe iye anachitira anthu ena. Iyeyu ananyoza Yehova, Woyera wa Israeli.
30 Aussi ses jeunes gens tomberont-ils sur ses places publiques, et tous ses combattants seront anéantis en ce jour, dit le Seigneur.
Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake; ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova.
31 Voici, je vais m’en prendre à toi, modèle d’arrogance, dit le Seigneur, Eternel-Cebaot; car ton jour est venu, l’époque pour te châtier.
“Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, “chifukwa tsiku lako lafika, nthawi yoti ndikulange yakwana.
32 Ce modèle d’arrogance trébuchera et tombera, sans personne pour le relever; je mettrai le feu à ses villes. et il dévorera tous ses alentours.
Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa ndipo palibe amene adzakudzutse; ndidzayatsa moto mʼmizinda yake umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
33 Ainsi parle l’Eternel-Cebaot: Opprimés sont les enfants d’Israël, et les enfants de Juda tous ensemble; tous ceux qui les ont réduits en captivité les retiennent de force, refusent de les relâcher.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a ku Israeli akuzunzidwa, pamodzi ndi anthu a ku Yuda, ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa, akukana kuwamasula.
34 Mais leur sauveur est puissantEternel-Cebaot est son nom, il prendra en mains leur cause, de façon à rendre la paix à la terre et à faire trembler les habitants de Babel.
Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo, koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
35 Guerre aux Chaldéens, dit le Seigneur, aux habitants de Babel, à ses princes et à ses sages!
Yehova akuti, “Imfa yalunjika pa Ababuloni, pa akuluakulu ake ndi pa anthu ake a nzeru!
36 Guerre aux trafiquants de mensonge! ils perdront la tête. Guerre à ses braves! ils seront brisés.
Imfa yalunjika pa aneneri abodza kuti asanduke zitsiru. Imfa yalunjika pa ankhondo ake kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
37 Guerre à ses coursiers, à ses chars et à tout ce ramassis de gens qu’elle abrite et qui deviendront comme des femmes! Guerre à ses trésors! Qu’ils soient pillés!
Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake. Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo kuti asanduke ngati akazi. Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake kuti chidzafunkhidwe.
38 Sécheresse sur ses eaux, pour qu’elles tarissent! car c’est un pays d’idoles, et on s’y targue follement de ces épouvantails.
Chilala chilunjike pa madzi ake kuti aphwe. Babuloni ndi dziko la mafano, ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
39 C’Est pourquoi chiens sauvages et chats sauvages s’y rencontreront, et des autruches en feront leur séjour: elle ne sera plus jamais habitée, jusqu’aux dernières générations personne ne s’y établira
“Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko ndipo kudzakhalanso akadzidzi. Kumeneko sikudzapezekako anthu, ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
40 Tel le bouleversement de Sodome, de Gomorrhe et de leurs environs, dit le Seigneur; aucun homme n’y habitera, nul mortel n’y séjournera.
Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,” akutero Yehova, “momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko; anthu sadzayendanso mʼmenemo.
41 Voici, une nation arrive du Nord, un grand peuple et des rois puissants surgissent des extrémités de la terre.
“Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri, wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
42 Ils sont armés d’arcs et de lances; ils sont inexorables et ne connaissent point la pitié. Leur voix est mugissante comme la mer; ils sont montés sur des chevaux, rangés en bataille comme des braves, contre toi, b fille de Babel.
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo. Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo, ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo iwe Babuloni.
43 Leur renommée est parvenue au roi de Babel, et ses mains sont devenues défaillantes; l’effroi s’est emparé de lui, une angoisse comme celle d’une femme qui enfante.
Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo, ndipo yalobodokeratu. Ikuda nkhawa, ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
44 Voici, tel un lion monte des rives escarpées du Jourdain contre les solides bergeries, en un clin d’oeil je délogerai les habitants de Babel de là, et j’y établirai comme maître celui que j’aurai choisi; car qui est mon égal? Qui m’appellera en justice? Quel est le pasteur qui tiendra ferme contre moi?
Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani kupita ku msipu wobiriwira, momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi. Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine. Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane? Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
45 Ecoutez donc les desseins de l’Eternel, qu’il a formés contre Babel et les projets qu’il a médités contre la terre des Chaldéens: certes, les plus humbles gardiens des troupeaux les traîneront dans la poussière, certes on fera s’écrouler sur eux leurs bergeries.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
46 Au bruit de la prise de Babel, la terre a frémi et une clameur se fait entendre parmi les nations.
Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera, ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.

< Jérémie 50 >