< Jérémie 46 >

1 Telle est la communication que l’Eternel fit à Jérémie concernant les nations.
Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
2 Au sujet de l’Egypte, en ce qui a trait à l’armée de Pharaon Nekho, roi d’Egypte, rassemblée près du fleuve de l’Euphrate, à Kharkhémich, et qui fut battue par Nabuchodonosor, roi de Babylone, dans la quatrième année du règne de Joïakim, fils de Josias, roi de Juda:
Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
3 "Armez-vous de boucliers et d’écus et marchez au combat!
anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
4 Attelez les chevaux, montez-les, cavaliers, présentez-vous, casques en tête; fourbissez vos lances, endossez vos cuirasses.
Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
5 Pourquoi les ai-je vus, frappés de terreur, battre en retraite? Leurs guerriers sont écrasés, ils fuient d’une fuite éperdue, sans se retourner: l’épouvante règne tout autour, dit l’Eternel.
Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
6 Non, il ne s’échappera point, le plus léger à la course, ni le plus vaillant ne pourra sauver sa vie; là, dans la région du Nord, sur les bords du fleuve de l’Euphrate, ils trébuchent, ils tombent.
Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
7 Qui est-ce donc qui est monté comme le Nil et dont les flots s’avancent tumultueux comme des torrents?
“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
8 C’Est l’Egypte qui est montée, pareille au Nil, et dont les eaux se sont précipitées en tumulte comme les torrents. Elle s’est écriée: Je vais monter, je vais inonder la terre, détruire les villes et ceux qui les habitent.
Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
9 Elancez-vous, ô coursiers, roulez, ô chars, paraissez, ô guerriers! Ceux de Couch et de Peut, qui portez le bouclier, Loudites, qui maniez et bandez l’arc!
Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
10 Ce jour appartient au Seigneur, à l’Eternel-Cebaot: c’est un jour de représailles pour tirer vengeance de ses ennemis. Le glaive dévorera à satiété et s’enivrera de leur sang. C’Est une hécatombe en l’honneur du Seigneur, Eternel-Cebaot, dans! e pays du Nord, sur les rives de l’Euphrate.
Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
11 Monte à Galaad et munis-toi de baume, ô vierge, fille d’Egypte! Tu as beau multiplier les remèdes, pour toi point de guérison.
“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
12 Les nations ont appris ta honte, la terre est remplie de tes cris de désespoir, car le guerrier a trébuché contre le guerrier, tous deux sont tombés du coup."
Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
13 Communication adressée par l’Eternel au prophète Jérémie; lorsque Nabuchodonosor, roi de Babylone, s’avançait pour abattre le pays d’Egypte:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
14 "Annoncez-le en Egypte, publiez-le à Migdol, publiez-le à Nof et à Tahpanhès, dites: Debout! Tiens-toi prêt! car le glaive dévore autour de toi.
“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
15 Pourquoi tes fiers combattants sont-ils violemment renversés? Pas un ne résiste; c’est que l’Eternel les a culbutés.
Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
16 Nombreux sont ceux qu’il fait trébucher, l’un se jette sur l’autre, disant: Allons, retournons parmi notre peuple et dans notre pays natal, pour échapper au glaive meurtrier.
Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
17 Là ils interpellent bruyamment Pharaon, roi d’Egypte: "Il a laissé passer le moment!"
Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
18 Aussi vrai que j’existe, dit le Roi, qui a nom Eternel-Cebaot, pareil au Thabor, parmi les montagnes, comme le Carmel qui s’avance dans la mer, il va venir, l’ennemi vainqueur.
“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
19 Prépare-toi une toilette d’exil, ô insouciante fille d’Egypte! car Nof deviendra une solitude, elle sera ruinée, dépeuplée.
Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
20 O Egypte, génisse aux belles formes, la calamité s’avance du Nord, elle s’avance.
“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
21 Même les mercenaires qu’elle abrite sont comme des veaux à l’engrais; eux aussi lâchent pied, s’enfuient ensemble, sans résister. C’Est que leur jour fatal est venu les atteindre, l’heure vengeresse.
Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
22 Son cri sera strident comme le sifflement du serpent, lorsque les ennemis marcheront contre elle, armés de haches comme des bûcherons.
Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
23 Ils abattent sa forêt, dit l’Eternel, elle si impénétrable cependant; c’est qu’ils sont plus nombreux que des sauterelles, on ne peut les compter.
Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
24 Elle est couverte de confusion, la fille de l’Egypte: elle a été livrée entre les mains d’un peuple du Nord.
Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
25 L’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël, a dit: Voici, je vais sévir sur Amon divinité de Nô, sur Pharaon et sur l’Egypte, sur ses dieux et ses rois, oui, sur Pharaon et sur ceux qui mettent leur confiance en lui.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
26 Je les livrerai à leurs mortels ennemis, à Nabuchodonosor et à ses serviteurs. Et après cela, ce pays sera habité comme dans les temps passés, dit l’Eternel.
Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
27 Pour toi, ô mon serviteur Jacob, ne crains rien; ne sois point alarmé, ô Israël! car mon secours te fera sortir des régions lointaines et tes descendants de leur pays d’exil. Jacob reviendra, et il jouira d’une paix et d’une sécurité que personne ne troublera.
“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
28 Non, toi, tu n’as rien à craindre, mon serviteur Jacob, dit l’Eternel, car je serai avec toi. Dussé-je détruire de fond en comble tous les peuples, parmi lesquels je t’aurai relégué, que toi, je ne te détruirais pas. Je te frapperai avec mesure, mais n’aurai garde de consommer ta ruine."
Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”

< Jérémie 46 >