< Jérémie 36 >

1 Dans la quatrième année du règne de Joïakim, fils de Josias, roi de Juda, la parole que voici fut adressée à Jérémie de la part de l’Eternel:
Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 "Prends un rouleau de parchemin et mets-y par écrit toutes les paroles que je t’ai adressées au sujet d’Israël, de Juda et de toutes les nations, depuis le jour où j’ai communiqué avec toi, à l’époque de Josias, jusqu’à ce jour.
“Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
3 Peut-être les gens de Juda tiendront-ils compte de tous les maux que j’ai dessein de leur infliger, pour qu’ils abandonnent leur voie pernicieuse et que je puisse pardonner leur iniquité et leurs fautes."
Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
4 Jérémie fit venir Baruch, fils de Néria, et celui-ci, sous la dictée de Jérémie, écrivit sur un rouleau de parchemin toutes les paroles que Dieu lui avait adressées.
Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
5 Puis Jérémie fit à Baruch la recommandation suivante: "Je suis retenu en prison et ne puis me rendre dans la maison de l’Eternel.
Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
6 Tu iras donc, toi, et, dans ce rouleau que tu as écrit sous ma dictée, tu liras les paroles de l’Eternel en présence du peuple, réuni dans la maison de l’Eternel à l’occasion d’un jour de jeûne. Tu les liras aussi en présence de tous les Judéens qui sont arrivés de leurs villes.
Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
7 Peut-être leurs supplications se répandront-elles devant l’Eternel, et chacun d’eux abandonnera-t-il sa voie pernicieuse; car grandes sont la colère et l’indignation dont l’Eternel a menacé ce peuple."
Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
8 Baruch, fils de Néria, se conforma fidèlement aux instructions de Jérémie, le prophète, en lisant au Temple les paroles de l’Eternel, consignées sur le livre.
Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
9 Dans la cinquième année du règne de Joïakim, fils de Josias, roi de Juda, au cours du neuvième mois, on convoqua pour un jeûne devant l’Eternel tous les habitants de Jérusalem et toute la population qui, des villes de Juda, s’était rendue à Jérusalem.
Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
10 Baruch lut alors, d’après son rouleau, les paroles de Jérémie, au Temple de l’Eternel, dans la salle de Ghemaria, fils du secrétaire Chafan, située dans la Cour supérieure, à l’entrée de la porte neuve du Temple. C’Était en présence de tout le peuple.
Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
11 Or, Mikhaïhou, fils de Ghemaria, fils de Chafan, ayant entendu toutes les paroles de l’Eternel, consignées sur le livre,
Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
12 descendit au palais du roi, dans la salle du secrétaire, où se trouvaient réunis tous les hauts fonctionnaires: Elichama, le secrétaire, Delaïa, fils de Chemaya, Elnathan, fils d’Akhbor, Ghemaria, fils de Chafan, Sédécias, fils de Hanania, et tous les seigneurs.
anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
13 Mikhaïhou leur rapporta toutes les paroles qu’il avait entendues, lorsque Baruch avait fait la lecture du livre en présence du peuple.
Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
14 Tous ces seigneurs dépêchèrent alors à Baruch lehoudi„ fils de Netania, fils de Chélémia, fils de Couchi, pour lui dire: "Ce rouleau que tu as lu à haute voix devant le peuple, emporte-le avec toi et viens." Baruch, fils de Néria, prit le rouleau dans sa main et se rendit auprès d’eux.
Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
15 Ils lui dirent: "Prends donc place, et fais-nous-en la lecture." Et Baruch le, lut devant eux.
Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
16 Lorsqu’ils entendirent toutes ces paroles, ils se regardèrent avec effroi les uns! es autres et dirent à Baruch: "Il faut que nous rapportions au roi toutes ces paroles!"
Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
17 Et ils interrogèrent Baruch en ces termes: "Dis-nous donc de quelle façon tu as écrit ces paroles sous sa dictée?"
Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
18 Baruch leur répondit: "Il me dictait de vive voix toutes ces paroles, et moi je les transcrivais avec de l’encre sur le livre."
Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
19 Les seigneurs dirent à Baruch: "Va te mettre en sûreté, toi ainsi que Jérémie; que personne ne sache où vous êtes!"
Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
20 Puis ils se rendirent à la Cour auprès du roi, après avoir déposé le rouleau dans la salle d’Elichama, le secrétaire, et ils racontèrent au roi tous ces faits.
Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
21 Le roi envoya chercher le rouleau par lehoudi, qui le retira de la salle d’Elichama, le secrétaire. Et lehoudi en donna lecture en présence du roi et en présence de tous les grands qui se tenaient debout devant le roi.
Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
22 Or, le roi était assis dans son appartement d’hiver (on était au neuvième mois), et devant lui il y avait un brasier allumé.
Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
23 A mesure que lehoudi achevait de lire trois ou quatre colonnes, le roi les détachait avec un canif de scribe et les jetait au feu dans le brasier, jusqu’à ce que tout le rouleau eût été ainsi consumé par le feu du brasier.
Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
24 Le roi et ses officiers qui avaient entendu toutes ces paroles n’en avaient éprouvé aucune crainte ni n’avaient déchiré leurs vêtements.
Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
25 Elnathan, Delaïa et Ghemaria avaient bien supplié le roi de ne pas brûler le rouleau, mais il ne les avait point écoutés.
Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
26 Le roi ordonna même à lerahmeêl, prince royal, à Seraïa, fils d’Azriel, et Chélémia, fils d’Abdiel, de se saisir de Baruch, le secrétaire, et de Jérémie, le prophète, mais l’Eternel les tint cachés.
Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
27 La parole de l’Eternel fut adressée à Jérémie, après que le roi eut brûlé le rouleau et les discours qu’y avait écrits Baruch sous la dictée de Jérémie.
Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
28 "Va, dit-il, prendre derechef un autre rouleau, et inscris-y toutes les paroles primitives qui figuraient sur le premier rouleau, brûlé par Joïakim, roi de Juda.
“Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
29 Et à propos de Joïakim, roi de Juda, tu diras: "Ainsi parle l’Eternel: Tu as jeté au feu ce rouleau en t’écriant: Pourquoi y as-tu inscrit ces mots: "A coup sûr, il viendra le roi de Babylone, il ruinera ce pays et en fera disparaître hommes et bêtes"?
Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
30 Eh bien! voici ce que décrète l’Eternel au sujet de Joïakim, roi de Juda: "Il n’aura point d’héritier siégeant sur le trône de David, et son cadavre se trouvera exposé à la chaleur du jour et au froid de la nuit.
Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
31 Je le châtierai, lui, sa race, ses officiers, pour leurs crimes, et je ferai fondre sur eux, sur les habitants de Jérusalem et les gens de Juda toutes les calamités que je leur ai annoncées, sans qu’ils voulussent écouter."
Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
32 Jérémie se munit donc d’un autre rouleau, qu’il remit à Baruch, fils de Néria, le secrétaire. Celui-ci écrivit, sous la dictée de Jérémie, toutes les paroles. inscrites dans le livre qu’avait livré au feu Joïakim, roi de Juda. Beaucoup d’autres paroles de même nature y furent encore ajoutées.
Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.

< Jérémie 36 >