< Isaïe 42 >

1 Voici mon serviteur, que je tiens par la main, mon élu, en qui mon âme se complaît; sur lui, j’ai répandu mon esprit, pour qu’il révèle aux nations ce qui est juste.
“Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
2 Il ne crie pas, n’élève pas la voix et ne fait pas entendre ses clameurs dans la rue.
Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
3 Il ne brise pas le roseau rompu, il n’éteint pas la mèche qui fume encore; c’est en toute vérité qu’il proclame le droit.
Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
4 Il ne se lassera ni se rebutera qu’il n’ait établi la justice sur la terre: les îles attendent sa doctrine.
sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
5 Ainsi parle le Tout-Puissant, l’Eternel qui a créé les cieux et les a déployés, qui a étalé la terre avec ses productions, qui donne la vie aux hommes qui l’habitent et le souffle à ceux qui la foulent:
Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
6 "Moi, l’Eternel, je t’ai appelé pour la justice et je te prends par la main; je te protège et je t’établis pour la fédération des peuples et la lumière des nations;
“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
7 pour dessiller les yeux frappés de cécité, pour tirer le captif de la prison, du cachot ceux qui vivent dans les ténèbres.
Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
8 Je suis l’Eternel, c’est mon nom! Je ne prête ma majesté à aucun autre, ni ma gloire à des idoles sculptées.
“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
9 Les prophéties anciennes, voilà, elles sont' accomplies; j’annonce des événements nouveaux, et avant qu’ils éclosent, je vous les fais connaître."
Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
10 Chantez à l’Eternel un chant nouveau, entonnez sa louange aux derniers confins du monde, voyageurs de la mer, êtres qui la peuplez, îles avec vos habitants!
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
11 Que le désert et ses villes élèvent la voix, ainsi que les bourgades où demeure Kédar; qu’ils chantent, les habitants des rochers, qu’ils poussent des cris de joie du sommet des montagnes!
Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
12 Qu’ils rendent hommage à l’Eternel, qu’ils proclament sa gloire dans les îles!
Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
13 L’Eternel s’avance comme un héros, comme un guerrier il réveille son ardeur; il fait éclater sa voix, il pousse le cri de guerre, il déploie sa puissance contre les ennemis.
Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
14 Depuis longtemps je reste calme, je garde le silence, je me contiens; mais maintenant je vais crier comme une femme en travail et tout détruire d’un souffle.
Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
15 Je vais calciner les montagnes et les coteaux et en flétrir toute la verdure, transformer les cours d’eau en îles et mettre à sec les étangs.
Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
16 Et je conduirai les aveugles dans une route à eux inconnue, et je les ferai cheminer dans des sentiers qu’ils ignorent; je convertirai pour eux les ténèbres en lumière et les aspérités en terrain uni… Ces choses-là, je les accomplis sans en rien omettre.
Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
17 Reculent maintenant et soient couverts de honte ceux qui se fient aux idoles de pierre, ceux qui disent à des idoles de fonte: "Vous êtes nos dieux!"
Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
18 Vous qui êtes sourds, entendez; aveugles, ouvrez les yeux et voyez!
“Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
19 Qui est aveugle, sinon mon serviteur, sourd, sinon le messager que j’envoie? Qui est aveugle comme le favori (du Seigneur), aveugle comme le serviteur de l’Eternel?
Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
20 Tu as vu de grandes choses et tu n’as pas fait attention, tu avais les oreilles ouvertes sans rien entendre!
Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
21 L’Eternel s’est complu, pour le triomphe de sa justice, à rendre sa doctrine grande et glorieuse.
Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
22 Et pourtant Israël est un peuple pillé et dépouillé: tous, on les a confinés dans des fosses et relégués dans des cachots; on les a spoliés et nul ne les a protégés, on a fait main basse et nul n’a dit: "Rendez gorge!"
Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
23 En est-il parmi vous qui veuille prêter son attention à cette leçon et s’appliquer à la comprendre dans l’avenir:
Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
24 Qui a livré Jacob au pillage et Israël à l’avidité des ravisseurs, si ce n’est l’Eternel? C’Est que nous avons péché contre lui: l’on a refusé de marcher dans ses voies, et l’on n’a pas obéi à sa doctrine.
Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
25 Alors il a lancé sur lui le feu de sa colère et la violence de la guerre. Des flammes l’ont enveloppé de toutes parts, et il n’a pas compris, l’incendie l’a touché, et il n’a pas pris la chose à cœur.
Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.

< Isaïe 42 >