< Isaïe 30 >
1 Malheur, enfants rebelles, dit le Seigneur, vous qui machinez des plans en dehors de moi, contractez des alliances contre mon gré et accumulez ainsi faute sur faute,
Yehova akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira amene amachita zowakomera iwo okha osati Ine, nachita mgwirizano wawowawo koma osati motsogozedwa ndi Ine. Choncho amanka nachimwirachimwira.
2 vous qui vous mettez en route pour descendre en Egypte, sans avoir demandé mon avis, avec l’espoir de trouver une force dans l’appui de Pharaon et un abri à l’ombre des Egyptiens!
Amapita ku Igupto kukapempha thandizo koma osandifunsa; amathawira kwa Farao kuti awateteze, ku Igupto amafuna malo opulumulira.
3 Mais l’appui de Pharaon sera votre honte, et l’abri à l’ombre des Egyptiens votre déshonneur.
Koma chitetezo cha Farao chidzakhala manyazi anu, malo a mthunzi a ku Igupto mudzachita nawo manyazi.
4 C’Est que déjà ses princes sont à Çoân, et ses messagers ont atteint Hanès.
Ngakhale kuti nduna zawo zili ku Zowani, ndipo akazembe awo afika kale ku Hanesi,
5 Mais tous seront déçus au sujet d’un peuple qui ne leur sera d’aucun secours, qui ne sera ni un appui ni une force, mais seulement une cause de déboire et même d’opprobre.
aliyense wa ku Yuda adzachita manyazi chifukwa cha anthu opanda nawo phindu, amene sabweretsa thandizo kapena phindu, koma manyazi ndi mnyozo.”
6 Oracle à propos des animaux du Midi: À travers un pays de détresse et d’angoisse, où vivent lions et lionnes, aspics et dragons volants, ils transportent sur la croupe des ânons leurs richesses, et sur le dos des chameaux leurs trésors, chez un peuple qui n’est d’aucun secours.
Uthenga wonena za nyama za ku Negevi: Akazembe akuyenda mʼdziko lovuta ndi losautsa, mʼmene muli mikango yayimuna ndi yayikazi, mphiri ndi njoka zaululu. Iwo amasenzetsa abulu ndi ngamira chuma chawo, kupita nazo kwa mtundu wa anthu umene sungawathandize.
7 L’Appui de l’Egypte, en effet, est vain et illusoire; aussi je dis de cette nation: "Ils font beaucoup de bruit, mais ils restent cois."
Amapita ku Igupto amene thandizo lake ndi lachabechabe. Nʼchifukwa chake dzikolo ndalitcha Rahabe chirombo cholobodoka.
8 Maintenant donc rentre, mets cela par écrit sur une tablette en leur présence, fixe-le sur un livre pour durer jusqu’au jour le plus reculé, toujours et toujours.
Yehova anandiwuza kuti, “Tsopano pita, ukalembe zimenezi mʼbuku iwo akuona ndipo lidzakhala ngati umboni wosatha masiku a mʼtsogolo.
9 Car c’est un peuple indocile, des enfants déloyaux, des enfants qui refusent d’entendre l’enseignement du Seigneur;
Amenewa ndi anthu owukira, onama ndi osafuna kumvera malangizo a Yehova.
10 Qui disent aux voyants: "Ne voyez point!" et aux prophètes: "Ne nous révélez pas de vérités! Débitez-nous des choses agréables; prophétisez de quoi nourrir nos illusions!
Iwo amawuza alosi kuti, ‘Musationerenso masomphenya!’ Ndipo amanena kwa mneneri kuti, ‘Musatinenerenso zoona,’ mutiwuze zotikomera, munenere za mʼmutu mwanu.
11 Eloignez-vous du chemin, détournez-vous de la route, laissez-nous en paix avec le Saint d’Israël!"
Patukani pa njira ya Yehova, lekani kutsata njira ya Yehova; ndipo tisamvenso mawu a Woyerayo uja wa Israeli!”
12 C’Est pourquoi le Saint d’Israël parle ainsi: "Puisque vous avez méprisé mes exhortations, placé votre confiance et cherché un appui dans la fraude et le mensonge,
Nʼchifukwa chake Woyerayo wa Israeli akunena kuti, “Popeza inu mwakana uthenga uwu, mumakhulupirira zopondereza anzanu ndipo mumadalira kuchita zoyipa,
13 ce crime sera pour vous tel qu’une lézarde menaçante, apparaissant dans un mur élevé qui s’écroule brusquement, en un instant,
choncho tchimo linalo lidzakhala ngati mingʼalu pa khoma lalitali ndi lopendama limene linagwa mwadzidzidzi ndi mwamsangamsanga.
14 et qui tombe en ruines comme on brise un vase de potiers, en l’écrasant sans pitié, de telle sorte que dans ses débris on ne peut même ramasser un tesson pour prendre du feu au foyer ou puiser de l’eau à la citerne."
Lidzaphwanyika ngati mbiya imene yanyenyekeratu, mwakuti pakati pake sipadzapezeka phale ngakhale lopalira moto mʼngʼanjo kapena lotungira madzi mʼchitsime.”
15 Car ainsi avait parlé le Seigneur, le Dieu éternel, le Saint d’Israël: "C’Est la paix et la douceur qui seront votre salut, la quiétude et la confiance qui seront votre force," mais vous vous y êtes refusés.
Zimene Ambuye Yehova, Woyerayo wa Israeli ananena ndi izi: “Ngati mubwerera ndi kupuma mudzapulumuka, ngati mukhala chete ndi kukhulupirira mudzakhala amphamvu, koma inu munakana zimenezi.
16 Vous disiez: "Non! Nous voulons galoper sur des chevaux," eh bien! Vous galoperez pour fuir "nous voulons monter des coursiers rapides," eh bien! Ils seront rapides, ceux qui courront après vous.
Inu mukuti, ‘Ayi ife tidzathawa, tidzakwera pa akavalo aliwiro.’ Zoonadi kuti mudzakwera pa akavalo aliwiro, koma okuthamangitsani adzakhalanso aliwiro.
17 Au nombre de mille, vous fuirez devant la menace d’un seul, devant la menace de cinq, de façon à vous trouver isolés comme un mât sur le sommet de la montagne, comme une bannière sur la hauteur.
Anthu 1,000 mwa inu adzathawa poona mdani mmodzi; poona adani asanu okha nonsenu mudzathawa. Otsala anu adzakhala ngati mbendera pa phiri, ndi ngati chizindikiro cha pa chulu.”
18 Pourtant, le Seigneur ne demande qu’à vous rendre sa faveur; pourtant, il se lèvera pour vous prendre en pitié, car le Seigneur est un Dieu de justice: heureux ceux qui espèrent en lui!
Komatu Yehova akufunitsitsa kuti akukomereni mtima, iye ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo. Pakuti Yehova ndi Mulungu wachilungamo. Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!
19 Oui, ô peuple de Sion, qui habites dans Jérusalem, tu ne pleureras pas toujours: il accueillera avec bienveillance ta voix suppliante; dès qu’il l’entendra, il te répondra.
Inu anthu a ku Ziyoni, amene mukhala mu Yerusalemu simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu kopempha thandizo! Ndipo akadzamva, adzakuyankhani.
20 Le Seigneur vous accordera du pain dans la détresse et de l’eau dans la pénurie; ton guide ne se dérobera plus à ton regard, tes yeux pourront voir ton guide,
Ngakhale Ambuye adzakulowetseni mʼmasautso, aphunzitsi anu sadzakhala kakasi; inu mudzawaona ndi maso anuwo.
21 et tes oreilles entendre ces paroles qui seront prononcées derrière toi "Voici la route! Suivez-la, que vous preniez à droite ou que vous preniez à gauche."
Ngati mudzapatukira kumanja kapena kumanzere, mudzamva mawu kumbuyo kwanu woti, “Njira ndi iyi; yendani mʼmenemo.”
22 Alors vous déclarerez impurs le revêtement de vos idoles d’argent et l’enveloppe de vos statues d’or, vous les rejetterez au loin comme des immondices: "Hors d’ici!" leur direz-vous.
Pamenepo mudzawononga mafano anu okutidwa ndi siliva ndiponso zifanizo zanu zokutidwa ndi golide; mudzawataya ngati zinthu zonyansa ndipo mudzati, “Zichoke zonsezi!”
23 Et Dieu dispensera la pluie à la semence que vous confierez au sol le pain que produira la terre sera substantiel et savoureux, tes troupeaux paîtront en ce jour dans de vastes prairies.
Yehova adzakugwetseraninso mvula pa mbewu zanu zimene mukadzale mʼnthaka, ndipo chakudya chimene mudzakolole chidzakhala chabwino ndi chochuluka. Tsiku limenelo ngʼombe zanu zidzadya msipu wochuluka.
24 Les bœufs et les ânes, employés aux travaux des champs, mangeront un fourrage assaisonné de sel et qu’on aura vanné avec la pelle et le van.
Ngʼombe ndi abulu amene amalima mʼmunda adzadya chakudya chamchere, chopetedwa ndi foloko ndi fosholo.
25 Sur toute haute montagne et sur toute colline élevée, il y aura des ruisseaux, des eaux courantes, au jour du grand massacre, lors de la chute des tours fortifiées.
Pa tsiku limene adani anu adzaphedwa ndi nsanja zawo kugwa, mitsinje ya madzi idzayenda pa phiri lililonse lalikulu ndi pa phiri lililonse lalingʼono.
26 La lune, alors, brillera du même éclat que le soleil, et la lumière du soleil sera sept fois plus vive, comme la lumière des sept jours, à l’époque où l’Eternel pansera les blessures de son peuple et guérira les meurtrissures qui l’ont atteint.
Mwezi udzawala ngati dzuwa, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzawonjezereka kasanu nʼkawiri, ngati kuwala kwa tsiku limodzi. Yehova adzamanga mabala a anthu ake ndi kupoletsa zilonda zimene Iye anachititsa polanga anthu ake.
27 Voici la majesté de l’Eternel qui s’avance de loin: ardente est sa colère, pesant le tourbillon de fumée qui s’élève, ses lèvres sont chargées de courroux, sa langue est comme un feu dévorant,
Taonani, Yehova akubwera kuchokera kutali, ndipo mkwiyo wake ndiwonyeka ndi chiweruzo chake chidzakhala chopweteka. Iye wayankhula mwaukali kwambiri, ndipo mawu ake ali ngati moto wonyeka.
28 son souffle comme un torrent impétueux qui monte jusqu’au cou: il va secouer les peuples dans le van de la destruction et poser entre les mâchoires des peuples un frein qui les dirige de travers.
Mpweya wake uli ngati mtsinje wosefukira, wa madzi ofika mʼkhosi. Iye adzasefa anthu a mitundu ina ndi sefa wosakaza; Iye akuyika zitsulo mʼkamwa mwa anthu a mitundu ina ngati akavalo, kuti ziwasocheretse.
29 Parmi vous retentiront des chants, comme dans la nuit consacrée à une fête; vous aurez le cœur joyeux comme les pèlerins qui, au son de la flûte, se rendent sur la montagne de l’Eternel auprès du rocher d’Israël.
Ndipo inu mudzayimba mokondwa monga mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika. Mudzasangalala ngati anthu oyimba zitoliro popita ku phiri la Yehova, thanthwe la Israeli.
30 Dieu fera éclater sa voix majestueuse et sentir la pesanteur de son bras qui s’abat, dans un déchaînement de colère, dans l’embrasement d’un feu dévorant, accompagné de tempêtes, de pluies violentes et de grêlons.
Anthu adzamva liwu la ulemerero la Yehova ndipo adzaona dzanja lake likutsika pa iwo ndi mkwiyo woopsa, pamodzi ndi moto wonyeketsa, mphenzi, namondwe ndi matalala.
31 Aussi à la voix de l’Eternel, Achour sera pris de terreur, tandis que Dieu le frappera de son bâton.
Asiriya adzaopa liwu la Yehova, ndipo Iye adzawakantha ndi ndodo.
32 Et chaque fois que retombera ce bâton prédestiné, que l’Eternel brandit contre lui, on entendra des tambourins et des harpes. Ce sont des combats acharnés que lui livrera Dieu.
Yehova akamadzalanga adani ake ndi ndodo, anthu ake adzakhala akuvina nyimbo zoyimbira matambolini ndi azeze, Yehova ndiye ati adzamenyane ndi Asiriyawo.
33 Car dès longtemps le Tofet est tout prêt; il a été disposé, lui aussi, profond et large, pour le roi, avec son bûcher allumé, où le bois abonde et que fait flamber le souffle de l’Eternel, tel qu’un torrent de soufre.
Malo otenthera zinthu akonzedwa kale; anakonzera mfumu ya ku Asiriya. Dzenje la motolo ndi lozama ndi lalikulu, ndipo muli nkhuni zambiri; mpweya wa Yehova, wangati mtsinje wa sulufule, udzayatsa motowo pa nkhunizo.