< Ézéchiel 9 >

1 Puis il cria à mes oreilles d’une voix forte, disant: "Approchez, fléaux de la ville, chacun son engin de destruction à la main."
Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
2 Et voici que six hommes venaient du côté de la porte supérieure qui regarde au Nord, chacun avec son engin de ruine à la main, et il y avait un homme au milieu d’eux, vêtu de lin, avec l’écritoire du scribe aux reins, et ils vinrent se poster près de l’autel de cuivre.
Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
3 Et la gloire du Dieu d’Israël s’éleva, de dessus le Chérubin sur lequel elle se trouvait, vers le seuil de la maison et appela l’homme vêtu de lin qui avait l’écritoire du scribe aux reins.
Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
4 L’Eternel lui dit: "Passe au milieu de la ville, au milieu de Jérusalem, et tu dessineras un signe sur le front des hommes qui soupirent et gémissent à cause de toutes les iniquités qui s’y commettent."
ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
5 Et aux autres il dit, à mes oreilles: "Passez dans la ville derrière lui, et frappez; que votre oeil n’ait pas d’indulgence et n’ayez pas pitié.
Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
6 Vieillards, jeunes gens et jeunes filles, enfants et femmes, tuez-les, détruisez-les, mais de tout homme qui porte le signe n’approchez pas, et commencez par mon sanctuaire. "Ils commencèrent par les hommes âgés qui étaient devant le temple."
Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
7 Et il leur dit: "Profanez la maison et remplissez les cours de cadavres; sortez!" Et ils sortirent et frappèrent dans la ville.
Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
8 Or, comme ils frappaient, et que je demeurais là, je tombai sur ma face, je criai et dis: "Hélas! Seigneur Dieu, vas-tu détruire tout ce qui reste d’Israël en épanchant ta colère sur Jérusalem?"
Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
9 Il me dit: "L’Iniquité de la maison d’Israël et de Juda est grande, très grande, le pays est rempli de sang, la ville est remplie de dénis de justice, car ils ont dit: "L’Eternel a délaissé le pays, l’Eternel ne voit pas."
Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
10 Moi non plus, mon oeil n’aura pas d’indulgence et je n’aurai pas de pitié, je ferai retomber leurs actes sur leur tête.
Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
11 "Et voici que l’homme, vêtu de lin, qui avait l’écritoire aux reins, fit son rapport en disant: "J’Ai agi comme tu m’avais commandé."
Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”

< Ézéchiel 9 >