< Ézéchiel 43 >
1 Puis, il me conduisit à la porte, à cette porte qui est disposée du côté de l’Est.
Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku chipinda choyangʼana kummawa,
2 Et voici que la gloire du Dieu d’Israël s’avançait du côté de l’Est; son grondement ressemblait au bruit de grandes eaux, et la terre s’illuminait de sa gloire.
ndipo ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ukubwera kuchokera kummawa. Liwu lake linali ngati mkokomo wamadzi, ndipo dziko linawala ndi ulemerero wake.
3 Cette vision était pareille à la vision qui m’était apparue, à la vision que j’avais eue en venant pour la destruction de la ville; c’étaient des visions comme celle que j’avais eue sur le fleuve de Khebar, et je tombai sur ma face.
Masomphenya amene ndinawaonawa anali ngati masomphenya amene ndinawaona pamene Yehova anabwera kudzawononga mzinda ndiponso ngati masomphenya amene ndinawaona ku mtsinje wa Kebara. Ndipo ndinadzigwetsa chafufumimba.
4 La gloire de l’Eternel entra dans le temple par la porte qui est tournée du côté de l’Est.
Ulemerero wa Yehova unalowa mʼNyumba ya Mulungu kudzera pa chipata choyangʼana kummawa.
5 Et l’esprit me souleva et m’amena dans le parvis intérieur, et voici que la gloire de l’Eternel remplissait le temple.
Tsono Mzimu unandinyamula nundilowetsa mʼbwalo lamʼkati, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
6 J’Entendis quelqu’un me parler du fond du temple, tandis que l’homme se tenait debout auprès de moi.
Munthuyo ali chiyimire pambali panga, ndinamva wina akundiyankhula kuchokera mʼNyumba ya Mulungu.
7 Il me dit: "Fils de l’homme, c’est ici l’emplacement de mon trône, le lieu où se pose la plante de mes pieds, où je résiderai à jamais au milieu des enfants d’Israël. Désormais la maison d’Israël ne profanera plus mon saint nomni eux, ni leurs roispar leurs prostitutions et les cadavres de leurs rois sur leurs hauts-lieux;
Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi malo a mpando wanga waufumu, ndi malo opondapo mapazi anga. Pano ndiye pamene ndidzakhala pakati pa Aisraeli mpaka muyaya. Aisraeliwa kapena mafumu awo sadzayipitsa dzina langa popembedza milungu ina kapena poyika mitembo ya mafumu awo ku zitunda zachipembedzo.
8 car ils mettaient leur seuil près de mon seuil, leurs poteaux près de mes poteaux, avec un simple mur entre moi et eux. C’Est ainsi qu’ils profanaient mon nom par les abominations qu’ils commettaient, et que je les ai consumés dans ma colère.
Ankamanga chiwundo chawo pafupi ndi chiwundo changa, ndiponso mphuthu zawo pafupi ndi mphuthu zanga, nʼkungokhala khoma chabe pakati pa iwowo ndi Ine. Motero anayipitsa dzina langa loyera ndi machitidwe awo onyansa. Choncho Ine ndinawawononga ndili wokwiya.
9 A présent, ils éloigneront de moi leurs prostitutions et les cadavres de leurs rois, et je résiderai parmi eux pour toujours.
Tsopano alekeretu kupembedza milungu ina ndipo achotseretu mitembo ya mafumu awo, isakhale pafupi ndi Ine, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo mpaka muyaya.
10 Toi, fils de l’homme, décris le temple à la maison d’Israël, pour qu’ils rougissent de leurs iniquités; qu’ils en vérifient le plan!
“Iwe mwana wa munthu, awuze Aisraeliwa za Nyumba ya Mulunguyi, mamangidwe ake ndipo achite manyazi ndi machimo awo,
11 S’Ils rougissent de tout ce qu’ils ont fait, expose-leur et dessine devant eux le plan du temple, ses dispositions, ses issues, ses accès, toutes ses parties, ses dimensions, sa forme et son ordonnance; qu’ils en retiennent tout le plan et l’architecture, afin de les exécuter.
akachita manyazi ndi zoyipa zonse anachita, uwafotokozera za Nyumba ya Mulungu, mamangidwe ake, makomo ake otulukira ndi makomo olowera, ndiye kuti, mamangidwe ake onse. Uwafotokozerenso malangizo ndi malamulo ake. Uwalembe akuona kuti athe kuwasunga ndi kuwachita.
12 Voici la règle relative au temple: situé sur le sommet de la montagne, tout son circuit à l’entour est éminemment saint. Telle est la règle relative au temple.
“Limeneli ndi lamulo la Nyumba ya Mulungu imene idzamangidwe pamwamba pa phiri. Malo ake onse ozungulira adzakhala oyera kwambiri. Limeneli ndilo lamulo la Nyumba ya Mulungu.
13 Et voici les dimensions de l’autel en coudées, chaque coudée valant une coudée et une palme: la cavité est d’une coudée de profondeur, plus une coudée de largeur, le rebord qui le limite à l’entour ayant un empan pour chaque face; tel est le support de l’autel.
“Miyeso ya guwa lansembe ndi iyi: Pa tsinde pake padzakhala ngalande ya masentimita makumi asanu kuzama kwake ndi mulifupi mwake. Mʼphepete mwa ngalandeyo kuzungulira guwa lonse, mudzakhala mkombero wa masentimita 25.
14 Depuis la cavité du sol jusqu’à la saillie inférieure, deux coudées; largeur, une coudée. Depuis la petite saillie jusqu’à la grande saillie, quatre coudées, sur une de largeur.
Kuchokera mʼngalande ya pansi padzakhala mpaka pa phaka lapansi mita imodzi, mulifupi mwake theka la mita. Kuchokera pa phaka lalingʼono mpaka pa phaka lalikulu, msinkhu wake ndi mamita awiri, mulifupi mwake ndi masentimita makumi asanu.
15 Pour le harêl, quatre coudées de hauteur, et au-dessus de l’ariêl s’élèvent les quatre cornes.
Malo osonkhapo moto pa guwa, msinkhu wake udzakhala mamita awiri. Pa ngodya iliyonse ya malo osonkhapo motowo panatuluka nyanga imodzi.
16 L’Ariêl, long de douze coudées sur douze de large, forme un carré par ses quatre côtés.
Malo osankhalapo moto pa guwa lansembe miyeso yake ndi yofanana mbali zonse. Mulitali mwake mudzakhala mamita asanu ndi limodzi ndipo mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi limodzi.
17 L’Enceinte a donc quatorze coudées de long sur quatorze de large, formant un carré par ses quatre côtés; le rebord qui le circonscrit a une demi-coudée, et la cavité intérieure une coudée en tous sens. Ses degrés sont dans la direction de l’Orient."
Phaka lapamwamba muyeso wake udzakhala wofanana mbali zonse. Mulitali mudzakhala mamita asanu ndi awiri ndiponso mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi awiri. Mkombero wake udzakhala wa masentimita 25 ndiponso ngalande yake yozungulira idzakhala ya masentimita 25. Makwerero a guwa lansembe adzayangʼana kummawa.”
18 Il me dit: "Fils de l’homme, ainsi parle le Seigneur Dieu: Voici quelles seront les règles de l’autel, du jour où il aura été construit: on y offrira des holocaustes et l’on y aspergera du sang.
Kenaka munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ambuye Yehova akuti: Guwalo litamangidwa, tsono malamulo awa azidzatsatidwa popereka nsembe zopsereza ndiponso powaza magazi pa guwapo.
19 Tu donneras aux pontifesaux Lévites qui sont de la lignée de Çadokqui s’approchent de moi, dit le Seigneur Dieu, pour me servir, un jeune taureau comme expiatoire.
Udzawapatse ansembe, omwe ndi Alevi, a banja la Zadoki, amene amabwera pafupi nane kudzanditumikira, mwana wangʼombe wamwamuna kuti aperekere nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
20 Tu prendras de son sang, que tu appliqueras aux quatre cornes, aux quatre angles de la saillie et tout autour du rebord; par là tu le purifieras et tu lui ôteras sa souillure.
Udzatengeko magazi ake ena ndi kuwapaka pa nyanga zinayi za pa guwa lansembe, pa ngodya zinayi za phaka ndiponso mozungulira mkombero wonse. Motero udzaliyeretsa ndi kulipatula.
21 Puis tu enlèveras ce taureau expiatoire, qu’on brûlera dans la dépendance du temple désignée pour cela, en dehors du sanctuaire.
Udzatenge ngʼombe yayimuna yomwe yaperekedwa ngati nsembe yopepesera machimo, ndipo udzayiwotche pa malo ake enieni mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, kunja kwa malo opatulika.
22 Le deuxième jour, tu offriras comme expiatoire un bouc sans défaut, et l’on purifiera l’autel comme on l’aura purifié par le taureau.
“Mmawa mwake udzatenge mbuzi yopanda chilema kuti nayonso iperekedwe ngati nsembe yopepesera machimo. Pambuyo pake idzayeretse guwa lansembe monga unachitira ndi ngʼombe yayimuna ija.
23 La purification terminée, tu présenteras un jeune taureau sans défaut et un bélier sans défaut choisi dans le menu bétail.
Utatha kuyeretsa guwa lansembelo, udzatenge mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndiponso nkhosa yayimuna yopanda chilema.
24 Tu les présenteras devant l’Eternel; les pontifes y répandront du sel et les offriront en holocauste à l’Eternel.
Udzapereke zonsezi pamaso pa Yehova, ndipo ansembe adzazithire mchere ndi kuzipereka kuti zikhale nsembe zopsereza kwa Yehova.
25 Sept jours durant, tu offriras chaque jour un bouc expiatoire; puis on offrira un jeune taureau et un bélier du menu bétail, on les offrira sans défaut.
“Kwa masiku asanu ndi awiri, uzidzapereka tsiku ndi tsiku mbuzi yayimuna, mwana wangʼombe, ndiponso nkhosa kuti zikhale nsembe zopepesera machimo. Zonsezi zidzakhale zopanda chilema.
26 On mettra sept jours à faire l’expiation de l’autel, à le purifier et à l’inaugurer.
Kwa masiku asanu ndi awiriwo ansembe adzachite mwambo woyeretsa ndi kupatula guwa lansembelo.
27 Quand on aura épuisé cette série de jours, c’est-à-dire à partir du huitième jour, les pontifes offriront sur l’autel vos holocaustes et vos rémunératoires, et je vous serai propice, dit le Seigneur Dieu."
Masiku amenewa atatha, kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu, ansembe azipereka nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe. Apo ndidzakulandirani. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”