< Ézéchiel 3 >

1 Et il me dit: "Fils de l’homme, mange ce que tu trouves là, mange ce rouleau et va parler à la maison d’Israël."
Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
2 J’Ouvris la bouche, et il me fit manger ce rouleau.
Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
3 Et il me dit: "Fils de l’homme, tu nourriras ton ventre' et rempliras tes entrailles de ce rouleau que je te donne"; je le mangeai et il devint dans ma bouche aussi doux que du miel.
Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
4 Il me dit encore: "Fils de l’homme, debout! Va auprès de la maison d’Israël et communique-leur mes paroles.
Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
5 Car ce n’est pas comme à un peuple à l’idiome obscur et à la langue lourde que tu es envoyé à la maison d’Israël.
Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
6 Ce n’est pas à des peuples nombreux au langage obscur et à la langue lourde, dont tu ne comprends pas les paroles; si à ceux-là je t’envoyais, eux, ils t’écouteraient.
Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
7 Mais la maison d’Israël ne consentira pas à t’écouter, car ils ne veulent pas m’écouter; car la maison d’Israël tout entière a le front rétif et le coeur endurci.
Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
8 Voici que je rendrai ton visage résolu en face de leurs visages et ton front résolu en face de leur front.
Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
9 Comme le diamant plus dur que le roc, je ferai ton front. Tu n’auras pas peur d’eux, tu ne trembleras pas à cause d’eux, parce qu’ils sont une maison de rébellion.
Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
10 Et il me dit: "Fils de l’homme, toutes les paroles que je te dirai, accueille-les dans ton coeur et écoute-les de tes oreilles.
Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
11 Et va-t-en trouver les exilés, les fils de ton peuple, et tu: leur diras: "Ainsi a parlé le Seigneur Dieu," soit qu’ils écoutent, soit qu’ils refusent."
Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
12 Et l’esprit m’emporta et j’entendis derrière moi le bruit d’un grand tumulte: "Bénie soit la gloire de l’Eternel en son lieu!"
Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
13 Et le bruit des ailes des Haïot qui se joignaient l’une l’autre et le bruit des roues vis-à-vis d’elles et le bruit d’un grand tumulte.
Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
14 Et l’esprit m’éleva en l’air et m’emporta, et je m’en allai, triste, dans l’exaltation de mon esprit, et la main du Seigneur pesait sur moi fortement.
Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
15 Et j’allai vers les exilés à Tel-Abib, vers ceux qui demeurent près du fleuve de Kebar, et là où ils étaient assis, je demeurai pendant sept jours, affligé, au milieu d’eux.
Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
16 Il advint au bout de sept jours que la parole du Seigneur me fut adressée en ces termes:
Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
17 "Fils de l’homme, je t’ai placé en sentinelle sur la maison d’Israël, tu écouteras ce que ma bouche dira, et tu les admonesteras de ma part.
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
18 Quand je dirai à l’impie: "Oui, tu mourras!" si tu ne l’as pas averti, si tu n’as pas parlé afin de détourner par tes exhortations le méchant de sa mauvaise voie et de sauver sa vie, le méchant mourra dans son iniquité, mais de son sang, je te demanderai compte.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
19 Mais si toi, tu avertis le méchant et qu’il ne revienne pas de son iniquité et de sa voie mauvaise, lui mourra dans son péché, et toi, tu auras la vie sauve.
Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
20 Et quand le juste se sera détourné de sa vertu pour faire le mal, je mettrai un obstacle devant lui et il mourra parce que tu ne l’auras pas averti, il mourra dans son péché et les actes de vertu qu’il a accomplis ne seront pas mentionnés, mais de son sang, je te demanderai compte.
“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
21 Mais que si toi tu avertis le juste pour que le juste ne pèche pas, et qu’en effet, il ne pèche pas, certes, il vivra, pour avoir été mis en garde, et toi, tu auras la vie sauve."
Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
22 Et la main du Seigneur fut sur moi en ce lieu et il me dit: "Lève-toi, sors vers la plaine et là je te parlerai"
Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
23 Et je me levai et je sortis vers la plaine, et voici que là se tenait la gloire de l’Eternel, comme la gloire que j’avais vue sur le fleuve de Kebar, et je tombai sur ma face.
Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
24 Et l’esprit vint en moi et me fit dresser sur mes pieds, et Dieu me parla et me dit: "Viens, enferme-toi dans ta maison.
Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
25 Et toi, fils de l’homme, voici qu’ils mettront sur toi des cordes avec lesquelles ils te lieront et tu ne sortiras pas parmi eux.
Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
26 Et j’attacherai ta langue à ton palais, tu deviendras muet, et tu ne leur seras pas un sermonneur, car ils sont une maison de rébellion.
Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
27 Mais quand je te parlerai, j’ouvrirai ta bouche et tu leur diras: "Ainsi parle le Seigneur Dieu: Ecoute qui veut écouter, refuse d’entendre qui veut refuser! Car ils sont une maison de rébellion!"
Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”

< Ézéchiel 3 >