< Ézéchiel 12 >
1 La parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 "Fils de l’homme, c’est au milieu de la maison de rébellion que tu demeures, chez ceux qui ont des yeux pour voir et n’ont pas vu, des oreilles pour entendre et n’ont pas entendu, car c’est une maison de rébellion.
“Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
3 Or toi, fils de l’homme, fais-toi des ustensiles d’exil et exile-toi, de jour, à leurs yeux; tu t’exileras de ta résidence vers une autre localité, à leurs yeux; peut-être s’en apercevront-ils, car ils sont une maison de rébellion.
“Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
4 Et, de jour, tu déposeras dehors tes ustensiles, comme des ustensiles d’exil, à leurs yeux, et toi-même tu sortiras, le soir, à leurs yeux, comme on part pour l’exil.
Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
5 A leurs yeux, creuse-toi un trou dans le mur et fais tout sortir par là.
Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
6 A leurs yeux, tu les porteras sur l’épaule, après les avoir fait sortir dans l’obscurité; tu te cacheras la face, pour ne pas voir la terre, car je fais de toi un symbole pour la maison d’Israël."
Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
7 Et je fis comme j’en avais reçu l’ordre, je fis sortir mes ustensiles comme des ustensiles d’exil, de jour, et, le soir, je me creusai un trou dans le mur, avec la main; dans l’obscurité, je les fis sortir et je les portai sur l’épaule, à leurs yeux.
Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
8 Et la parole de l’Eternel me fut adressée le matin, en ces termes:
Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
9 "Fils de l’homme, ne t’ont-ils pas dit, ceux de la maison d’Israël, de la maison de rébellion: Que fais-tu?
“Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
10 Réponds-leur: Ainsi parle le Seigneur Dieu: c’est pour le prince, cette prédiction, à Jérusalem, et pour toute la maison d’Israël qui s’y trouve.
“Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
11 Dis-leur: Je suis votre symbole; comme j’ai fait, ainsi il leur sera fait, ils iront en exil, en captivité.
Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
12 Et le prince qui est au milieu d’eux portera ses ustensiles sur l’épaule dans l’obscurité et sortira; on fera un trou dans le mur pour le faire sortir par là; il se couvrira la face, en sorte qu’il ne verra pas de ses yeux la terre.
“Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
13 Et j’étendrai mon filet sur lui et il sera pris dans mon panneau, et je le mènerai à Babylone, dans le pays des Chaldéens, mais il ne la verra pas et il y mourra.
Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
14 Et tous ceux qui l’entourent, sa garde et toutes ses troupes, je les disséminerai à tous les vents et je tirerai le glaive derrière eux.
Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
15 Ils sauront ainsi que je suis l’Eternel, quand je les disperserai parmi les nations et que je les disséminerai dans les pays.
“Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
16 Et je conserverai un petit nombre d’entre eux échappés au glaive, à la famine et à la peste, afin qu’ils racontent toutes leurs abominations chez les peuples où ils viendront, et ils sauront que je suis l’Eternel."
Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
17 La parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
18 "Fils de l’homme, ton pain, tu le mangeras avec tremblement, et ton eau, tu la boiras avec frisson et angoisse.
“Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
19 Et tu diras au peuple du pays: Ainsi parle le Seigneur Dieu aux habitants de Jérusalem, au pays d’Israël: leur pain, ils le mangeront avec angoisse, et leur eau, ils la boiront dans la stupeur, de façon que le pays soit désolé privé de son abondance, à cause de la violence de tous ses habitants.
Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
20 Les villes habitées seront dévastées et le pays sera une solitude, et vous saurez que je suis l’Eternel."
Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
21 La parole de Dieu me fut adressée en ces termes:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
22 "Fils de l’homme, quel est ce dicton que vous proférez là en terre d’Israël: "Les jours s’allongent et toute vision s’évanouit?"
“Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
23 C’Est pourquoi, dis-leur: Ainsi parle le Seigneur Dieu: J’Abolis ce dicton; on ne s’en servira plus en Israël; mais dis-leur au contraire: Les jours sont proches, et toute prophétie s’accomplira;
Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
24 car il n’y aura plus du tout de prophétie mensongère, ni d’oracle fallacieux dans la maison d’Israël.
Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
25 Car c’est moi, I’Eternel qui dirai la parole que je veux dire, et qui s’accomplira sans être plus différée, mais c’est de vos jours, maison de rébellion, que je dirai la parole que j’exécuterai, dit le Seigneur Dieu."
Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
26 La parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
Yehova anandiyankhula nati:
27 "Fils de l’homme, voici que la maison d’Israël dit: La vision qu’il perçoit concerne une époque reculée, c’est pour des temps éloignés qu’il prophétise.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
28 C’Est pourquoi, dis-leur: Ainsi parle le Seigneur Dieu: Aucune de mes paroles ne comporte plus de délai; va, toute parole que je prononce s’accomplira," dit le Seigneur Dieu.
“Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”