< Deutéronome 31 >

1 Moïse alla ensuite adresser les paroles suivantes à tout Israël,
Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
2 leur disant: "J’Ai cent vingt ans aujourd’hui, je ne peux plus vous servir de guide; d’ailleurs, l’Éternel m’a dit: "Tu ne traverseras pas ce Jourdain."
“Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
3 L’Éternel, ton Dieu, marche lui-même devant toi; c’est lui qui anéantira ces peuples devant toi pour que tu les dépossèdes. Josué sera ton guide, comme l’Éternel l’a déclaré.
Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
4 Et le Seigneur les traitera comme il a traité Sihôn et Og, rois des Amorréens, et leur pays, qu’il a condamné à la ruine.
Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
5 Il mettra ces peuples à votre merci; et vous procéderez à leur égard, en tout, selon l’ordre que je vous ai donné.
Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
6 Soyez forts et vaillants! Ne vous laissez effrayer ni intimider par eux! Car l’Éternel, ton Dieu, marche lui-même avec toi; il ne te laissera pas succomber, il ne t’abandonnera point!"
Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
7 Alors Moïse appela Josué, et lui dit en présence de tout Israël: "Sois fort et vaillant! Car c’est toi qui entreras avec ce peuple dans le pays que l’Éternel a juré à leurs pères de leur donner, et c’est toi qui leur en feras le partage.
Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
8 L’Éternel lui-même marchera devant toi, lui-même sera à tes côtés, il ne te laissera fléchir ni ne t’abandonnera: sois donc sans peur et sans faiblesse!"
Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
9 Moïse mit par écrit cette doctrine et la confia aux pontifes, descendants de Lévi, chargés de porter l’arche d’alliance du Seigneur, et à tous les anciens d’Israël.
Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
10 Et Moïse leur ordonna ce qui suit: "A la fin de chaque septième année, à l’époque de l’année de relâche, lors de la fête des tentes,
Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
11 alors que tout Israël vient comparaître devant l’Éternel, ton Dieu, dans l’endroit qu’il aura élu, tu feras lecture de cette doctrine en présence de tout Israël, qui écoutera attentivement.
pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
12 Convoques-y le peuple entier, hommes, femmes et enfants, ainsi que l’étranger qui est dans tes murs, afin qu’ils entendent et s’instruisent, et révèrent l’Éternel, votre Dieu, et s’appliquent à pratiquer toutes les paroles de cette doctrine;
Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
13 et que leurs enfants, qui ne savent pas encore, entendent aussi, et qu’ils apprennent à révérer l’Éternel, votre Dieu, tant que vous vivrez sur le sol pour la possession duquel vous allez passer le Jourdain."
Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
14 Le Seigneur dit à Moïse: "Voici que tes jours approchent de leur terme. Appelle Josué, et présentez-vous dans la tente d’assignation, pour que je lui donne mes ordres." Et Moïse alla, avec Josué, se placer dans la tente d’assignation.
Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
15 Le Seigneur apparut dans la tente, par une colonne de nuée, et cette colonne de nuée s’arrêta à l’entrée de la tente.
Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
16 Le Seigneur dit à Moïse: "Tandis que tu reposeras avec tes pères, ce peuple se laissera débaucher par les divinités du pays barbare où il va pénétrer; et il m’abandonnera, et il brisera l’alliance que j’ai conclue avec lui.
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
17 Ce jour-là, ma colère s’enflammera contre lui, je les abandonnerai, je leur déroberai ma face, et il deviendra la pâture de chacun, et nombre de maux et d’angoisses viendront l’assaillir. Alors il se dira: "En vérité, c’est parce que mon Dieu n’est plus au milieu de moi que je suis en butte à ces malheurs."
Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
18 Mais alors même, je persisterai, moi, à dérober ma face, à cause du grave méfait qu’il aura commis en se tournant vers des dieux étrangers.
Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
19 Et maintenant, écrivez pour vous ce cantique, qu’on l’enseigne aux enfants d’Israël et qu’on le mette dans leur bouche, afin que ce cantique me serve de témoignage à l’encontre des enfants d’Israël.
“Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
20 Quand j’aurai introduit ce peuple dans le pays que j’ai promis par serment à ses pères et où ruissellent le lait et le miel; vivant dans l’abondance et gorgé de délices, il s’adressera à des dieux étrangers, il les servira, me témoignera du mépris et rompra mon alliance.
Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
21 Vienne alors la multitude de maux et d’angoisses qui doivent l’atteindre, le présent cantique portera témoignage en face de lui (car la bouche de sa postérité ne l’oubliera point), parce que je sais ce qu’aujourd’hui déjà son penchant le porte à faire, avant même que je l’aie introduit dans la terre par moi promise!"
Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
22 Et Moïse écrivit le cantique suivant, ce jour même, et le fit apprendre aux enfants d’Israël.
Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
23 Et l’Éternel donna ses ordres à Josué, fils de Noun, et lui dit: "Sois ferme et courageux! Car c’est toi qui introduiras les Israélites dans la terre que je leur ai promise, et moi je t’assisterai."
Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
24 Or, lorsque Moïse eut achevé de transcrire les paroles de cette loi sur un livre, jusqu’au bout,
Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
25 il ordonna aux Lévites, porteurs de l’arche d’alliance du Seigneur, ce qui suit:
analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
26 "Prenez ce livre de la loi et déposez-le à côté de l’arche d’alliance de l’Éternel, votre Dieu; il y restera comme un témoin contre toi.
“Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
27 Car je connais ton indocilité et ton caractère obstiné: certes, si, moi vivant encore, étant avec vous à cette heure, vous vous êtes insurgés contre l’Éternel, que sera-ce après ma mort!
Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
28 Faites réunir autour de moi tous les anciens de vos tribus et vos magistrats: je veux faire parvenir ces paroles à leurs oreilles, et prendre à témoin contre eux les cieux et la terre.
Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
29 Car je sais qu’après ma mort vous irez dégénérant, et que vous dévierez du chemin que je vous ai prescrit; mais il vous arrivera malheur dans la suite des temps, pour avoir fait ce qui déplaît au Seigneur, pour l’avoir offensé par l’œuvre de vos mains!"
Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
30 Et Moïse fit entendre à toute l’assemblée d’Israël les paroles du cantique suivant, jusqu’à la fin:
Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:

< Deutéronome 31 >