< Daniel 6 >

1 Il parut bon à Darius de préposer au royaume cent vingt préfets, pour gouverner tout le royaume.
Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
2 Au-dessus d’eux il y avait trois ministres, dont était Daniel; c’est à eux que ces préfets devaient rendre des comptes, en sorte que le roi ne subît aucun dommage.
ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
3 Bientôt ce Daniel prit le dessus sur les ministres et les préfets, étant doué d’un esprit supérieur, et le roi projetait de le mettre à la tête de tout le royaume.
Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
4 Alors les ministres et les préfets s’appliquèrent à trouver un grief contre Daniel, du chef de son gouvernement, mais ils ne purent découvrir ni grief, ni méfait, parce qu’il était loyal, de sorte que ni erreur ni faute ne purent être surprises chez lui.
Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
5 Aussi ces hommes-là dirent: "Nous ne trouverons aucun grief contre ce Daniel, à moins que nous ne le prenions en défaut dans les choses de sa religion."
Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
6 Aussitôt les ministres et les préfets se précipitèrent chez le roi et lui parlèrent ainsi: "Vive à jamais le roi Darius!
Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
7 Tous les ministres du royaume, les préfets, les satrapes, les conseillers et les gouverneurs se sont concertés pour faire établir une ordonnance royale et promulguer une défense déclarant que quiconque, durant trente jours, adresserait une prière à tout autre Dieu ou homme qu’à toi-même, ô roi, serait jeté dans la fosse aux lions.
Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
8 Donc, ô roi, établis la défense et rédige l’édit qui ne puisse être modifié, conformément à la loi immuable de Médie et de Perse."
Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
9 En conséquence, le roi Darius rédigea l’édit et la défense.
Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
10 Or, Daniel, dès qu’il apprit que l’édit avait été rédigé, rentra chez lui. II avait, dans sa chambre supérieure, des fenêtres ouvertes dans la direction de Jérusalem, et trois fois par jour il se mettait à genoux, priant et louant Dieu tout comme il avait fait auparavant.
Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
11 Cependant, ces mêmes hommes se précipitèrent et surprirent Daniel priant et implorant son Dieu.
Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
12 Aussitôt ils se présentèrent devant le roi et l’entretinrent de la défense royale: "N’As-tu pas dirent-ils édicté une défense en vertu de laquelle tout homme qui, durant trente jours, adresserait une prière à tout autre Dieu ou homme que toi-même, ô roi, serait jeté dans la fosse aux lions?" Le roi répondit: "La chose est constante, conformément à la loi immuable de Médie et de Perse."
Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
13 Et eux de répliquer sur-le-champ au roi: "Daniel, qui fait partie des exilés de Judée, n’a tenu aucun compte de toi, ô roi, ni de la défense que tu as rédigée: trois fois par jour, il fait sa prière."
Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
14 Dès que le roi entendit ces paroles, il en fut très peiné, et il prit à cœur de tirer Daniel d’affaire: jusqu’au coucher du soleil il avisa aux moyens de le sauver.
Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
15 Mais alors ces gens firent irruption chez le roi et lui dirent: "Sache, ô roi, qu’une loi exige chez les Mèdes et les Perses que toute défense et tout édit établis par le roi soient immuables."
Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
16 Là-dessus, le roi donna un ordre, on amena Daniel et on le jeta dans la fosse aux lions: "Puisse, lui dit le roi, ton Dieu que tu sers constamment te sauver!"
Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
17 On apporta une pierre et on la posa sur l’orifice de la fosse; le roi la scella de son anneau et des anneaux de ses grands, pour qu’il n’y eût aucun revirement à l’égard de Daniel.
Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
18 Ensuite, le roi rentra dans son palais et passa la nuit en jeûnant; il ne fit pas dresser la table devant lui, et le sommeil s’obstina à le fuir.
Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
19 Dès l’aube, quand le jour vint à poindre, le roi se leva et se rendit en toute hâte à la fosse aux lions.
Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
20 Arrivé près de la fosse, il appela Daniel d’une voix attristée: "Daniel, serviteur du Dieu vivant, s’écria le roi en s’adressant à Daniel, ton Dieu que tu sers constamment a-t-il pu te préserver des lions?"
Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
21 Aussitôt Daniel parla au roi: "Vive, dit-il, le roi à jamais!
Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
22 Mon Dieu a envoyé son ange et fermé la gueule des lions, en sorte qu’ils ne m’ont fait aucun mal, parce que mon innocence a été reconnue par lui, de même qu’envers toi je n’ai commis aucun méfait."
Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
23 Alors le roi fut extrêmement content, et il ordonna de remonter Daniel de la fosse aux lions. Quand Daniel eut été remonté de la fosse, il ne portait aucune blessure, parce qu’il avait eu confiance en son Dieu.
Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
24 Puis, sur l’ordre du roi, on amena les hommes qui avaient dénoncé Daniel, et on les jeta dans la fosse aux lions, eux, leurs enfants et leurs femmes. Ils n’étaient pas encore arrivés au fond de la fosse, que les lions se jetèrent sur eux et leur broyèrent tous les membres.
Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
25 Alors le roi Darius manda à l’ensemble des nations, peuples et langues qui sont répandus sur toute la terre: "Que votre prospérité soit grande!
Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
26 L’Ordre est donné par moi que dans toute l’étendue de mon royaume on manifeste crainte et vénération pour le Dieu de Daniel car il est le Dieu vivant, et il subsiste éternellement; sa royauté est indestructible et sa dénomination sans fin.
“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
27 Il préserve et il sauve, il accomplit des miracles et des prodiges au ciel et sur la terre, lui qui a sauvé Daniel de la griffe des lions."
Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
28 Et ce même Daniel prospéra sous le règne de Darius et sous le règne de Cyrus le Perse.
Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.

< Daniel 6 >