< Daniel 11 >

1 Or moi, dès la première année de Darius le Mède, j’étais à mon poste pour lui servir de soutien et d’appui.
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 Maintenant je vais t’annoncer la vérité: voici, encore trois rois vont s’élever en Perse; puis le quatrième acquerra plus de richesses que tous les autres, et quand il se sentira fort par ses richesses, il mettra tout en mouvement contre le royaume de Grèce.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 Alors un roi guerrier s’élèvera, dominant sur un grand empire et agissant à son gré.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 Mais, quand il aura atteint le faite, son empire sera brisé et disloqué vers les quatre vents du ciel, sans passer à ses descendants ni conserver une puissance égale à la sienne. En effet, son empire sera démembré et réparti entre d’autres, à l’exclusion de ceux-là.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 Le roi du midi deviendra fort, ainsi que l’un de ses officiers; celui-ci sera encore plus fort que celui-là et prédominera: grande sera l’étendue de son empire.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 Au bout de quelques années ces dynasties s’allieront; la fille du roi du midi viendra chez le roi du nord pour rétablir l’harmonie; mais elle ne conservera pas l’avantage du pouvoir, son influence ne se maintiendra pas, et successivement elle sera livrée, elle et ceux qui l’auront amenée, de même que son père et son soutien.
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 De la même souche de racines d’où elle sera sortie elle-même montera un rejeton à sa place; il marchera contre l’armée syrienne et entrera dans la forteresse du roi du nord: il leur infligera des pertes et remportera la victoire.
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 Jusqu’à leurs Dieux et leurs dignitaires, avec leurs vases de prix en argent et en or, il les emmènera captifs en Egypte. Puis, pendant quelques années, il se tiendra à l’écart du roi du nord.
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 Celui-ci envahira le royaume du roi du sud, mais retournera en son pays.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 Mais ses fils reprendront les hostilités, ils rassembleront une grande multitude de troupes, qui viendront tout submerger sur leur passage; revenant à la charge, elles porteront la guerre jusque dans la forteresse.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 Puis le roi du sud, exaspéré, se mettra en campagne pour combattre contre le roi du nord, et réunira une nombreuse armée, et cette armée sera placée sous sa direction.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 Et l’armée sera puissante, et son cœur, à lui, s’enorgueillira: il fera tomber des myriades, mais ne triomphera pas longtemps.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 Ensuite, le roi du nord derechef lèvera une grande armée, plus nombreuse que la précédente, et au bout d’un certain temps, de quelques années, il se présentera avec de grandes forces et un puissant appareil.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 En ce temps-là, beaucoup s’élèveront contre le roi du sud, et des enfants scélérats de ton peuple s’insurgeront pour réaliser la vision, mais ils succomberont.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 Le roi du nord viendra donc, il élèvera des redoutes et s’emparera d’une ville forte; les forces du sud, pas même ses troupes d’élite, ne tiendront ferme; on n’aura pas d’énergie pour résister.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 L’Auteur de cette invasion agira à sa guise, personne ne pourra lui tenir tête; il prendra position dans le pays qui est le joyau des pays, apportant la ruine dans sa main.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 Il prendra ses dispositions pour venir avec toute la puissance de son royaume; mais il aura l’idée de faire un accord; il lui donnera une de ses filles en vue d’amener sa ruine, mais ce projet n’aura pas de suite et ne lui réussira pas.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 Il portera ses vues sur les provinces maritimes et en conquerra beaucoup; mais un capitaine mettra un terme à ses outrages, bien plus, il les fera retomber sur lui.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 De là il se dirigera vers les forteresses de son pays, mais il trébuchera et tombera, et c’en sera fini de lui.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 A sa place s’élèvera un roi qui enverra un exacteur dans la plus belle partie du royaume; mais en peu de jours il sera brisé, non par un mouvement de colère ni par la guerre.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 A sa place s’élèvera un homme méprisable, auquel on n’aura pas conféré la majesté royale; mais il viendra quand tout sera tranquille et s’emparera de la royauté par de basses intrigues.
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 Les armées venues comme une inondation seront submergées devant lui et brisées, de même qu’un prince de l’alliance.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 A la suite d’une convention qu’on aura faite avec lui, il agira avec perfidie; il entrera en campagne et sera victorieux avec peu de monde.
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 En pleine paix, il envahira les plus fertiles provinces et fera ce que n’auront fait ni ses pères ni ses aïeux: il leur prodiguera butin, prises et richesses; il forgera des plans contre des forteresses, mais pour un temps seulement.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 Il réveillera sa force et sa hardiesse contre le roi du sud, avec l’appui d’une grande armée, et le roi du sud entrera en guerre avec une armée extrêmement nombreuse et forte, mais il ne tiendra pas bon, car on usera d’intrigues à son égard.
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 Ses propres commensaux le briseront, son armée se débandera, et il tombera beaucoup de victimes.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 Quant aux deux rois, leur cœur nourrira de mauvais desseins: assis à une même table, ils se parleront avec fausseté; mais leur plan ne réussira pas, car la fin sera encore retardée pour un temps.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 Puis, il se dirigera vers son pays avec de grandes richesses; il formera des projets contre l’alliance sainte, les exécutera, et retournera dans son pays.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 Au temps marqué, il envahira de nouveau le sud, mais cette dernière expédition ne sera pas comme la première.
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 Des vaisseaux de Kittîm viendront contre lui, et il sera découragé; il rebroussera chemin et exercera sa fureur contre l’alliance sainte, puis il s’en retournera et sera d’intelligence avec les déserteurs de l’alliance sainte.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 Des troupes à lui demeureront et profaneront le sanctuaire, ce boulevard protecteur; elles supprimeront l’holocauste perpétuel et établiront l’abomination horrible.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 Ceux qui seront traîtres à l’alliance, il les séduira par des promesses fallacieuses, mais les gens qui connaissent leur Dieu resteront fermes et agiront.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 Les sages parmi le peuple en éclaireront beaucoup, mais pendant un certain temps ils succomberont par le glaive et la flamme, par l’exil et le pillage.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 Pendant leurs revers, ils recevront un peu d’aide, et un grand nombre se rallieront à eux d’une façon hypocrite.
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 Et du parti des sages, certains tomberont, pour qu’ils soient éprouvés, triés et purifiés en attendant le moment final, car il tardera encore, jusqu’à l’époque fixée.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 Le roi en fera à sa volonté; il se montrera altier et hautain contre toute divinité, et contre le Dieu des dieux il proférera des paroles inouïes. Tout lui réussira jusqu’à ce que la colère divine soit épuisée; car l’arrêt prononcé aura été exécuté.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 Il n’aura pas d’égards pour le Dieu de ses pères; il ne fera nulle attention à la divinité qui fait les délices des femmes, ni à aucun Dieu; car il se croira supérieur à tout.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Mais il honorera le Dieu des forteresses maritimes au centre de son culte, et un Dieu que n’avaient pas connu ses pères, il l’honorera par de l’or, de l’argent, des pierres précieuses et de rares trésors.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 Il agira dans l’intérêt des villes fortes en même temps que d’un Dieu étranger; quiconque adorera celui-ci, il le comblera d’honneurs, le mettra à la tête d’un grand nombre et distribuera des territoires comme récompense.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 Mais au temps final, le roi du sud entrera en collision avec lui, et le roi du nord fondra sur lui avec des chars, des cavaliers et quantité de vaisseaux; il envahira les territoires et submergera tout sur son passage.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 Il envahira aussi le pays, joyau des pays, et de grandes multitudes succomberont. Et voici ceux qui échapperont à ses coups: Edom, Moab et la région extrême des fils d’Ammon.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 Il étendra la main sur différents pays, et le pays d’Egypte ne sera pas à l’abri de ses atteintes.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 Il se rendra maître des trésors d’or et d’argent et de tous les objets précieux de l’Egypte; Libyens et Ethiopiens marcheront à sa suite.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 Mais des nouvelles de l’orient et du nord viendront le bouleverser, et il se retirera en grande fureur pour exterminer et ruiner des multitudes.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 Il dressera les tentes de son royal campement entre la mer et la montagne de la gloire sainte; mais il arrivera à son dernier jour, et personne ne viendra à son aide.
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”

< Daniel 11 >