< 2 Rois 9 >
1 Or, Elisée avait mandé un des jeunes prophètes pour lui dire: "Ceins tes reins, prends cette fiole d’huile en ta main et rends-toi à Ramot-Galaad.
Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
2 Arrivé à destination, enquiers-toi de Jéhu, fils de Josaphat, fils de Nimchi. Une fois admis en sa présence, tu l’engageras à se lever du milieu de ses frères d’armes et l’introduiras dans une chambre retirée.
Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
3 Prends alors la fiole d’huile, répands-la sur sa tête en disant: Ainsi a parlé l’Eternel: Je te sacre roi d’Israël. Puis ouvre la porte et enfuis-toi sans retard."
Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
4 Le jeune homme, le jeune prophète, alla à Ramot-Galaad.
Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
5 Dès son arrivée, il trouva les chefs de l’armée siégeant ensemble, et il dit: "J’Ai une communication pour toi, ô commandant. Pour qui d’entre nous tous?" demanda Jéhu. "Pour toi, commandant," répondit-il.
Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
6 Jéhu se leva, entra dans la chambre, et le prophète lui versa l’huile sur la tête en lui disant: "Ainsi a parlé l’Eternel, le Dieu d’Israël: Je te sacre roi du peuple de l’Eternel, d’Israël.
Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
7 Tu frapperas la maison de ton maître Achab, et ainsi je vengerai sur Jézabel le sang de mes serviteurs les prophètes et le sang de tous les serviteurs du Seigneur.
Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
8 Toute la maison d’Achab doit périr: j’exterminerai la plus vile créature appartenant à Achab, tout ce qu’il possède de précieux et d’infime en Israël.
Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
9 Je ferai ainsi de la maison d’Achab ce que j’ai fait de la maison de Jéroboam, fils de Nebat, et de la maison de Baasa, fils d’Ahiyya.
Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
10 Quant à Jézabel, les chiens la dévoreront sur le domaine de Jezreël, et personne ne l’ensevelira." Puis il ouvrit la porte et s’enfuit.
Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
11 Jéhu sortit pour rejoindre les serviteurs de son maître. On lui demanda: "Tout est-il bien? Pourquoi cet exalté est-il venu te trouver?" Il leur répondit: "Vous connaissez bien l’homme et ses discours.
Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
12 —C’Est de la dissimulation, répliquèrent-ils; de grâce, raconte-nous tout." Il repartit: "C’Est de telle et telle façon qu’il m’a parlé; il m’a dit: Ainsi a parlé l’Eternel: Je te sacre roi d’Israël."
Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
13 Aussitôt ils s’empressèrent tous de prendre leurs manteaux, les étendirent sous lui au haut de l’escalier, et sonnèrent du cor en s’écriant: "Jéhu est roi!"
Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
14 C’Est de la sorte que Jéhu, fils de Josaphat, fils de Nimchi, complota contre Joram. Celui-ci avait été en observation à Ramot-Galaad, avec tout Israël, en face de Hazaël, roi de Syrie.
Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
15 Mais le roi Joram s’en était retourné pour attendre à Jezreël la guérison des blessures que lui avaient faites les Syriens au cours de sa campagne contre Hazaël, roi de Syrie. Jéhu dit: "Si vous le voulez bien, qu’aucun transfuge ne sorte de la ville pour porter des nouvelles à Jezreël."
koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
16 Jehu monta sur son char et se rendit à Jezreël, où Joram était alité. Achazia, roi de Juda, était descendu pour rendre visite à Joram.
Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
17 Or, le gardien qui se tenait sur la tour de Jezreël remarqua la troupe de Jéhu qui avançait, et il dit: "J’Aperçois une troupe." Joram répliqua: "Prends un cavalier, dépêche-le au-devant d’eux pour qu’il demande: Est-ce la paix?"
Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
18 Le cavalier se rendit au-devant de Jéhu et dit: "Voici ce que demande le roi: Est-ce la paix?" Jéhu répondit: "Quoi de commun entre toi et la paix? Passe derrière moi." La sentinelle en fit part en disant: "Le messager est arrivé jusqu’à eux, mais n’est point revenu."
Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
19 Il envoya un second cavalier, qui, arrivé auprès d’eux, dit: Voici ce que demande le roi: Est-ce la paix?" Jéhu répondit: "Quoi de commun entre toi et la paix? Passe derrière moi."
Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
20 La sentinelle en fit part en ces termes: "Il est arrivé jusqu’à eux et n’est point revenu. Or, le train ressemble au train de Jéhu, fils de Nimchi; car il dirige d’une manière désordonnée."
Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
21 Joram dit: "Attelle!" On attela son char, et Joram, roi d’Israël, Achazia, roi de Juda, chacun sur son char, sortirent à la rencontre de Jéhu. Ils le joignirent près du domaine de Nabot, le Jezreélite.
Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
22 Dès que Joram aperçut Jéhu, il dit: "Est-ce la paix, Jéhu?" Peut-il être question de paix, fut la réponse, tant que durent les débordements de ta mère Jézabel et ses nombreux sortilèges?"
Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
23 Joram tourna bride et prit la fuite, en disant à Achazia: "Trahison, Achazia!"
Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
24 Jéhu saisit l’arc de sa main, et la flèche atteignit Joram entre les épaules, de façon à transpercer son cœur: il s’affaissa dans son char.
Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
25 Jéhu dit à Bidkar, son officier: "Enlève son corps et jette-le à terre dans le champ de Nabot, le Jezreélite; car je me souviens avec toi du jour où nous chevauchions de concert à la suite d’Achab, son père, alors que l’Eternel a émis contre lui cette prédiction:
Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
26 A coup sûr, j’ai remarqué hier le sang de Nabot et le sang de ses enfants (dit l’Eternel); je t’en paierai le prix dans ce champ même (dit l’Eternel); enlève-le donc et jette-le dans ce champ, conformément à la parole du Seigneur."
‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
27 A cette vue, Achazia, roi de Juda, se mit à fuir dans la direction de la maison du parc; Jéhu se lança à sa poursuite et dit: "Lui aussi, frappez-le!" Il fut atteint dans son char, sur la montée de Gour du côté de Yibleam. Il se réfugia à Meghiddo et y mourut.
Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
28 Ses serviteurs le transportèrent à Jérusalem et l’ensevelirent dans son sépulcre, auprès de ses aïeux, dans la Cité de David.
Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
29 (C’Était dans la onzième année de Joram, fils d’Achab, qu’Achazia avait commencé à régner sur Juda.)
(Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
30 Puis Jéhu entra à Jezreël. Or, Jézabel avait tout appris: elle s’enduisit les yeux de fard, se para la tête et regarda par la fenêtre.
Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
31 Jéhu franchissant la porte, elle s’écria: "Est-ce la paix, Zimri, assassin de ton maître?"
Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
32 Il leva les regards vers la fenêtre: "Qui est avec moi, qui?" dit-il. Deux ou trois officiers tournèrent les yeux vers lui,
Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
33 et il leur dit: "Précipitez-la!" Ils la précipitèrent. Son sang rejaillit sur le mur et sur les chevaux, et il la foula aux pieds.
Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
34 Il pénétra dans la ville, mangea et but; puis il dit: "Voyez donc après cette maudite et ensevelissez-la, puisqu’elle est fille de roi.
Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
35 Ils allèrent pour l’ensevelir, mais ne trouvèrent plus d’elle que le crâne, les pieds et les paumes des mains.
Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
36 Ils revinrent lui en faire part. Alors il s’écria: "Ainsi s’accomplit cette parole de l’Eternel, énoncée par la bouche de son serviteur, Elie le Tisbite: Sur le domaine de Jezreël, les chiens dévoreront la chair de Jézabel,
Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
37 et le cadavre de Jézabel sera étendu sur le domaine de Jezreël, pareil au fumier qui couvre les champs, de telle sorte qu’on ne puisse pas dire: C’Est là Jézabel!"
Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”