< 2 Chroniques 23 >
1 La septième année, Joïada prit courage et s’attacha par un pacte les centeniers Azaria, fils de Yeroham, Ismaël, fils de Johanan, Azariahou, fils d’Obed, Maassêyahou, fils d’Adaïahou, et Elichafat, fils de Zikhri.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
2 Ceux-ci parcoururent Juda en tout sens et rassemblèrent, de toutes les villes de Juda, les Lévites et les chefs de famille d’Israël, qui se rendirent à Jérusalem.
Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
3 Toute cette assemblée conclut un accord avec le roi dans la maison de Dieu, et Joïada leur dit: "Voici le fils du roi; il doit régner, selon la promesse faite par l’Eternel au sujet des descendants de David.
msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
4 C’Est ainsi que vous procéderez: un tiers d’entre vous, de ceux qui prennent la semaine en qualité de prêtres et de Lévites, gardera les entrées,
Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
5 un tiers surveillera la maison du roi, et un tiers, la porte de Yessod; et tout le peuple restera dans les cours de la maison de l’Eternel.
ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
6 Ainsi n’entreront dans le temple de l’Eternel que les prêtres et ceux qui font le service en qualité de Lévites; eux, ils peuvent entrer, car ils sont consacrés; quant au peuple tout entier, il doit respecter l’ordonnance de l’Eternel.
Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
7 Les Lévites feront cercle autour du roi, les armes à la main; quiconque voudra pénétrer dans le temple sera mis à mort. Vous accompagnerez le roi dans toutes ses démarches."
Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
8 Les Lévites et tout Juda exécutèrent fidèlement les ordres donnés par Joïada, le prêtre; ils prirent chacun leurs hommes, ceux qui commençaient et ceux qui avaient fini la semaine, car Joïada, le prêtre, n’avait pas congédié les sections.
Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
9 Le prêtre Joïada délivra aux centeniers les lances, les boucliers et autres armes ayant appartenu au roi David et déposées dans le temple de Dieu,
Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
10 et il rangea tout le peuple, armes en main, en partant du côté droit jusqu’au côté gauche du temple, de façon à entourer le roi.
Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
11 Puis, on fit sortir le fils du roi, on lui remit la couronne et le "témoignage"; on le proclama roi, Joïada et ses fils l’oignirent, et l’on cria "Vive le roi!"
Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
12 Athalie, entendant les cris du peuple qui accourait et acclamait le roi, se rendit au milieu de la foule dans le temple de l’Eternel.
Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
13 Elle regarda et vit ce spectacle: le roi debout sur son estrade à l’entrée, les chefs et les trompettes acclamant le roi, toute la foule manifestant sa joie en sonnant de la trompette, et les chanteurs, qui s’accompagnaient d’instruments de musique, donnant le signal des applaudissements. A cette vue, Athalie déchira ses vêtements et s’écria: "Trahison, trahison!"
Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
14 Le prêtre Joïada fit avancer les centeniers qui commandaient les troupes et leur dit: "Faites-la sortir des rangs, et qui la suivra, qu’on l’exécute avec le glaive!" Car le pontife avait recommandé qu’elle ne fût pas mise à mort dans la maison de l’Eternel.
Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
15 On fit place devant elle, et elle prit le chemin de l’entrée des chevaux pour se rendre au palais royal; là, on la mit à mort.
choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
16 Joïada conclut un pacte l’engageant lui, tout le peuple et le roi, à devenir le peuple de l’Eternel.
Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
17 Toute la foule pénétra dans le temple de Baal et le saccagea; on brisa ses autels et ses statues, on tua devant les autels Matân, prêtre de Baal.
Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
18 Le pontife plaça des surveillants dans la maison de l’Eternel, sous la direction des prêtres et des Lévites que David avait répartis en sections dans le temple du Seigneur, avec mission d’offrir les holocaustes à l’Eternel, conformément aux prescriptions de la Loi de Moïse, avec des manifestations de joie et des chants, selon le mode établi par David.
Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
19 Il disposa aussi les portiers près des portes du temple de l’Eternel pour en interdire l’accès à toute personne devenue impure par une cause quelconque.
Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
20 Il se fit accompagner par les centeniers, les notables, les principaux chefs du peuple et toute la population et conduisit le roi hors de la maison de l’Eternel; on entra dans le palais du roi, en franchissant la porte Supérieure, et on fit asseoir le roi sur le trône de la royauté.
Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
21 Tous les habitants du pays furent heureux, et la ville retrouva le calme. Quant à Athalie, on l’avait fait mourir par le glaive.
ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.