< 1 Samuel 21 >

1 David arriva à Nob, chez le prêtre Ahimélec. Celui-ci courut à sa rencontre et lui dit: "D’Où vient que tu es seul et que personne ne t’accompagne?"
Davide anapita ku Nobi kwa wansembe Ahimeleki. Ahimelekiyo ankanjenjemera pamene ankamuchingamira, ndipo anafunsa kuti, “Muli nokha chifukwa chiyani? Chifukwa chiyani mulibe wokuperekezani?”
2 "Le roi, lui répondit David, m’a donné une mission et m’a dit: Que personne ne sache rien de la mission et de l’ordre que je te donne. Quant aux serviteurs, je leur ai donné rendez-vous à certaine place.
Davide anayankha Ahimeleki kuti, “Mfumu yandituma zinthu zina ndipo yandiwuza kuti, ‘Munthu aliyense asadziwe za zimene ndakutumazo.’ Kunena za anthu anga, ndawawuza kuti tikakumane pamalo pena pake.
3 Et maintenant, ce que tu as sous la main, donne-le moi, cinq pains, ou n’importe quoi."
Kodi muli ndi chakudya? Patseniko malofu a buledi asanu, kapena chilichonse muli nacho.”
4 Le prêtre dit à David "Je n’ai pas de pain ordinaire sous la main, seulement du pain consacré, pourvu que tes serviteurs se soient tenus éloignés des femmes."
Koma wansembeyo anamuyankha Davide kuti, “Ine ndilibe buledi wamba woti ndikupatseni. Koma pali buledi wachipembedzo yekha. Ngati anthu amene muli nawo sanagone ndi akazi awo mukhoza kudya.”
5 "Certes, répondit David au prêtre, nulle femme n’était à notre portée, depuis environ deux ou trois jours que je suis parti, et les vases des serviteurs sont restés purs. S’Il en est ainsi par rapport aux choses profanes, à plus forte raison aujourd’hui que les vases doivent servir à un objet consacré"
Davide anayankha kuti, “Kunena zoona sitinakhudzane ndi mkazi monga timachitira nthawi zonse tikakhala pa ulendo. Anthu anga salola kudziyipitsa ndi mkazi ngakhale pa ulendo wamba. Nanji lero tili pa ulendo woterewu!”
6 Le prêtre lui donna donc du pain sacré, car il n’y en avait pas d’autre que les pains de proposition, qu’on enlevait de devant le Seigneur, pour y substituer, le jour même, du pain frais.
Choncho wansembe uja anamupatsa buledi wachipembedzo popeza kunalibeko buledi wina aliyense koma yekhayo amene amaperekedwa kwa Yehova. Uyu ndi amene anachotsedwa tsiku limenelo kuti ayikepo wina wotentha.
7 Or, là se trouvait, en ce moment, un des serviteurs de Saül, retenu en présence du Seigneur; son nom était Doëg l’Iduméen, intendant des troupeaux de Saül.
Koma tsiku limenelo mmodzi wa antchito a Sauli anali pomwepo kudikirira kuti achite mwambo wa chipembedzo mʼnyumba ya Mulungu. Munthuyu dzina lake anali Doegi Mwedomu, munthu wamphamvu pakati pa abusa a Sauli.
8 David dit à Ahimélec: "N’As-tu pas ici sous la main quelque lance ou épée? Je n’ai emporté ni mon épée ni mes autres armes, car l’ordre du roi était pressant."
Davide anafunsa Ahimeleki kuti, “Kodi muli ndi mkondo kapena lupanga pano? Ine sindinatenge lupanga langa kapena chida china chilichonse chifukwa zimene andituma amfumu ndi zamsangamsanga.”
9 Le prêtre répondit: "L’Épée de Goliath, le Philistin, que tu as vaincu dans la vallée du Térébinthe, est là, derrière l’éphod, enveloppée dans un drap. Prends-la si tu veux, car il n’y en a point d’autre ici. Elle n’a pas sa pareille, répliqua David, donne-la moi."
Wansembeyo anayankha kuti, “Kuno kuli lupanga la Goliati Mfilisiti uja amene unamupha mʼchigwa cha Ela, lakulungidwa mʼnsalu paseli pa Efodi. Ngati mufuna kulitenga, tengani popeza kuno kulibe lina koma lokhalo.” Davide anati, “Palibe lina lofanana nalo. Ndipatseni lomwelo.”
10 David se leva le jour même, toujours fuyant devant Saül et il se rendit chez Akhich, roi de Gath.
Tsiku lomwelo Davide ananyamuka kuthawa Sauli ndipo anapita kwa Akisi, mfumu wa ku Gati.
11 Les serviteurs d’Akhich lui dirent: "N’Est-ce pas là David, le roi du pays? N’Est-ce pas celui-là même qu’on acclamait dans les chœurs, en disant "Saül a battu ses milliers, Et David ses myriades"?
Koma nduna za Akisi zinafunsa mfumuyo kuti, “Kodi uyu si Davide mfumu ya dzikoli? Kodi iyeyu si uja pomuvinira ankayimba kuti, “Sauli wapha 1,000, koma Davide wapha miyandamiyanda?”
12 David prit ces propos à cœur et eut grandement peur d’Akhich, roi de Gath.
Mawu amenewa anamulowa kwambiri Davide mu mtima ndipo anayamba kuopa kwambiri Akisi mfumu ya ku Gati.
13 Alors il changea sa manière d’être en leur présence, en contrefaisant le fou au milieu d’eux; il traça des dessins sur les battants de la porte, et laissa la salive se répandre sur sa barbe.
Choncho anasintha makhalidwe ake pamaso pawo, nʼkudzisandutsa ngati wamisala. Iye ankangolembalemba pa zitseko za chipata ndi kumangotuluka dovi, nʼkumayenderera mʼndevu zake.
14 Et Akhich dit à ses serviteurs: "Vous voyez bien que cet homme a perdu la raison; pourquoi le faites-vous venir chez moi?
Akisi anawuza nduna zake kuti, “Mukumuona munthu uyu kuti ndi wamisala! Nʼchifukwa chiyani mukubwera naye kwa ine?
15 N’Ai-je pas assez de fous, sans que vous ameniez celui-ci pour se livrer à ses actes de folie devant moi? Un tel homme devait-il venir dans ma maison?"
Kodi ine ndikusowa anthu amisala kuti muzibwera naye munthuyu kwa ine kuti azidzachita zamisala zake pamaso panga? Kodi munthu ameneyu nʼkulowa mʼnyumba mwanga?”

< 1 Samuel 21 >