< 1 Rois 4 >

1 Le roi Salomon régna donc sur tout Israël.
Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
2 Et voici quels furent ses fonctionnaires: Azaryahou, fils de Çadok, le pontife:
Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
3 Elihoref et Ahiyya, fils de Chicha, secrétaires; Josaphat, fils d’Ahiloud, archiviste;
Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
4 Benaïahou, fils de Joïada, chef de l’armée; Çadok et Ebiathar, prêtres;
Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
5 Azaryahou, fils de Nathan, surintendant; Zaboud, fils de Nathan; prêtre, conseiller intime du roi;
Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
6 Ahichar, préposé au palais, et Adoniram, fils d’Abda, à l’impôt.
Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
7 Douze intendants représentaient Salomon en Israël, chargés de l’entretien du roi et de sa maison; chacun d’eux remplissait cette charge pendant un mois de l’année.
Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
8 Et voici leurs noms: Ben-Hour, exerçant sa fonction dans la montagne d’Ephraïm;
Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
9 Ben-Déker, à Mâquaç, à Schaalbim, à Bêth-Chémech et à Elôn-bêth-Hanan;
Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
10 Ben-Héced, à Aroubbot, gouvernant Sokho et tout le canton de Hêfer;
Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
11 Ben-Abinadab, ayant toute la région de Dor (il avait épousé Tafat, fille de Salomon);
Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
12 Baana, fils d’Ahiloud, à Taanakh, à Meghiddo, et dans tout Bêth-Cheân, qui est près de Çarethân, au-dessous de Jezreël, depuis Bêth-Cheân jusqu’à la plaine de Mehola et jusqu’au delà de Yokmeâm;
Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
13 Ben-Ghéber, à Ramot-Galaad, avait les bourgs de Jaïr, fils de Manassé, qui sont situés en Galaad; il avait aussi le district d’Argob, dans le Basan, comprenant soixante grandes villes, avec murailles et verrous d’airain;
Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
14 Ahinadab, fils d’Iddo, à Mahanaïm;
Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
15 Ahimaaç, en Nephtali; il avait, lui aussi, épousé une fille de Salomon, Basmat;
Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
16 Baana, fils de Houchaï, en Aser et à Bealot;
Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
17 Josaphat, fils de Parouah, en Issachar;
Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
18 Séméi, fils d’Ela, en Benjamin;
Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
19 Ghéber, fils d’Ouri, au pays de Galaad, territoire de Sihôn, roi des Amorréens, et d’Og, roi du Basan; il y avait un seul intendant pour cette contrée.
Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
20 Juda et Israël étaient nombreux comme les grains de sable de l’Océan; on mangeait, on buvait et on était tout à la joie.
Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
21 Salomon avait autorité sur tous les pays situés entre le Fleuve et le pays des Philistins, jusqu’à la frontière d’Egypte; ils lui apportaient des présents et lui restèrent soumis toute sa vie durant.
Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
22 L’Entretien de Salomon exigeait chaque jour: trente kôr de fleur de farine et soixante kôr de farine commune;
Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
23 dix bœufs engraissés, vingt de libre pâture et cent pièces de menu bétail, sans compter les cerfs, chevreuils, daims et volailles grasses.
ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
24 Car il commandait à tout le pays en deçà du Fleuve et à tous les rois de cette région, depuis Tifsah jusqu’à Gaza, et était en paix avec tous ses voisins d’alentour.
Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
25 Juda et Israël, pendant toute la vie de Salomon, demeurèrent en sécurité, chacun sous sa vigne et sous son figuier, depuis Dan jusqu’à Bersabée.
Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
26 Salomon avait quarante mille attelages de chevaux pour ses chars et douze mille chevaux de selle.
Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
27 Les intendants en question, chacun dans son mois, pourvoyaient le roi Salomon et tous ceux qui étaient admis à sa table, sans les laisser manquer de rien.
Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
28 L’Orge et la paille destinées aux chevaux et autres montures, ils les amenaient, chacun selon sa consigne, à l’endroit où se trouvait le roi.
Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
29 Or, Dieu avait donné à Salomon un très haut degré de sagesse et d’intelligence, et une compréhension aussi vaste que le sable qui est au bord de la mer.
Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
30 La sagesse de Salomon était plus grande que celle de tous les Orientaux, plus grande que toute la sagesse des Egyptiens.
Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
31 Plus savant que tout homme, plus qu’Ethan l’Ezrahite, que Hêman, Kalkol et Darda, les fils de Mahol, sa renommée s’étendit chez tous les peuples voisins.
Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
32 Il composa trois mille paraboles, mille cinq poésies;
Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
33 discourut sur les végétaux, depuis le cèdre du Liban jusqu’à l’hysope qui rampe sur la muraille; discourut sur les quadrupèdes, les oiseaux, les reptiles et les poissons.
Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
34 On venait de chez tous les peuples pour se rendre compte de la sagesse de Salomon, de la part de tous les rois de la terre qui avaient entendu parler de sa sagesse.
Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.

< 1 Rois 4 >