< 1 Chroniques 28 >

1 David rassembla à Jérusalem tous les chefs d’Israël, les chefs des tribus, les chefs des sections, chargés du service du roi, les chiliarques, les centurions, les intendants de tous les biens et troupeaux appartenant au roi et à ses fils, en même temps que les fonctionnaires du palais, les héros et tous les vaillants guerriers.
Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
2 Se mettant debout, le roi David dit: "Ecoutez-moi, mes frères, mon peuple! J’Avais à cœur, moi, de bâtir une résidence stable pour l’arche d’alliance de l’Eternel et le marche-pied de notre Dieu, et j’avais fait des préparatifs pour cette construction.
Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
3 Mais Dieu m’a dit: "Ce n’est pas toi qui bâtiras une maison en l’honneur de mon nom, car tu es un homme de guerre, et tu as répandu du sang!"
Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
4 Or, l’Eternel, Dieu d’Israël, m’a donné la préférence sur toute la maison de mon père pour régner à jamais sur Israël, car, ayant élu Juda comme prince et choisi, dans la tribu de Juda, la maison de mon père, c’est moi des fils de mon père qu’il a agréé pour me faire roi de tout Israël.
“Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
5 Et entre tous mes fils car le Seigneur m’a donné de nombreux fils il a choisi mon fils Salomon pour occuper le trône de la royauté de l’Eternel en Israël.
Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
6 Il m’a dit: "C’Est ton fils Salomon qui bâtira ma maison et mes parvis, car je l’ai choisi pour m’être un fils, et moi, je lui servirai de père.
Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
7 Je consoliderai sa royauté à jamais, pourvu qu’il persévère à observer mes préceptes et mes lois comme en ce jour."
Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
8 Et maintenant, en présence de tout Israël, de cette assemblée du Seigneur, et de notre Dieu, qui nous entend, je vous dis: "Respectez et pratiquez tous les préceptes de l’Eternel, votre Dieu, afin de demeurer en possession de ce beau pays et de le transmettre à vos fils après vous comme un héritage éternel."
“Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
9 Quant à toi, mon fils Salomon, reconnais le Dieu de ton père et adore-le d’un cœur intègre et d’une âme empressée, car le Seigneur sonde tous les cœurs et pénètre tout dessein des pensées: si tu le recherches, il te sera accessible, mais si tu l’abandonnes, il te délaissera pour toujours.
“Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
10 Considère maintenant que c’est toi que l’Eternel a choisi pour construire une maison comme sanctuaire: courage donc et à l’œuvre!"
Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
11 David remit alors à son fils Salomon le plan du portique, des bâtisses du temple, de ses salles de dépôt, de ses chambres supérieures, de ses salles intérieures et de l’enceinte du propitiatoire;
Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
12 le plan de tout ce qu’il avait projeté concernant les parvis du temple de l’Eternel, toutes les salles du pourtour, les trésors du temple de Dieu et les trésors des choses saintes;
Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
13 les sections des prêtres et des Lévites, toute l’organisation du service de la maison de l’Eternel et tous les ustensiles destinés au service de la maison de l’Eternel;
Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
14 le plan de tous les objets en or, en indiquant le poids en or de tous les ustensiles nécessaires à chaque service; de même, de tous les ustensiles en argent, en indiquant le poids de tous les ustensiles nécessaires à chaque service.
Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
15 Il remit aussi le poids en or pour les chandeliers d’or et leurs lampes d’or, en tenant compte du poids de chaque chandelier et de ses lampes, et pour les chandeliers d’argent, le poids pour chaque chandelier et ses lampes, suivant la destination de chaque chandelier;
kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
16 le poids en or pour chacune des tables de proposition et l’argent pour les tables d’argent;
kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
17 l’or pur pour les fourchettes, les bassins et les montants; le poids d’or nécessaire pour chacune des écuelles d’or et le poids d’argent nécessaire pour chacune des écuelles d’argent:
muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
18 le poids d’or affiné pour l’autel des parfums. Il remit aussi le plan du char, des chérubins d’or ayant les ailes étendues et recouvrant l’arche d’alliance du Seigneur,
ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
19 "Tout cela disait David tous les détails du plan est consigné par écrit, tel que l’inspiration de l’Eternel me l’a fait connaître."
Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
20 Le roi David dit à son fils Salomon: "Sois fort et vaillant, et mets-toi à l’œuvre! Sois sans peur et sans faiblesse! Car l’Eternel-Dieu, mon Dieu, sera avec toi; il ne te laissera fléchir ni ne t’abandonnera jusqu’à l’achèvement de tout le travail du service de la maison de l’Eternel.
Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
21 Voici, d’ailleurs, les sections des prêtres et des Lévites, chargés de tout le service de la maison de Dieu; pour chaque ouvrage, tu seras secondé par des hommes de bonne volonté, experts en tout travail. De plus, les chefs et tout le peuple seront à ta disposition pour toutes tes entreprises."
Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”

< 1 Chroniques 28 >