< Psaumes 97 >

1 L’Éternel règne: que la terre s’égaie, que les îles nombreuses se réjouissent!
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Des nuées et l’obscurité sont autour de lui; la justice et le jugement sont la base de son trône.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Un feu va devant lui et consume à l’entour ses adversaires.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Ses éclairs illuminent le monde: la terre le vit et trembla.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Les montagnes se fondirent comme de la cire, à la présence de l’Éternel, à la présence du Seigneur de toute la terre.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Les cieux déclarent sa justice, et tous les peuples voient sa gloire.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Que tous ceux qui servent une image taillée, qui se vantent des idoles, soient honteux. Vous, tous les dieux, prosternez-vous devant lui.
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Sion l’a entendu, et s’est réjouie; et les filles de Juda se sont égayées à cause de tes jugements, ô Éternel!
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Car toi, Éternel! tu es le Très-haut sur toute la terre; tu es fort élevé par-dessus tous les dieux.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Vous qui aimez l’Éternel, haïssez le mal! Il garde les âmes de ses saints, il les délivre de la main des méchants.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 La lumière est semée pour le juste, et la joie pour ceux qui sont droits de cœur.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Justes, réjouissez-vous en l’Éternel, et célébrez la mémoire de sa sainteté!
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.

< Psaumes 97 >