< Psaumes 90 >

1 Prière de Moïse, homme de Dieu. Seigneur, tu as été notre demeure de génération en génération.
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
2 Avant que les montagnes soient nées et que tu aies formé la terre et le monde, d’éternité en éternité tu es Dieu.
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 Tu fais retourner l’homme jusqu’à la poussière, et tu dis: Retournez, fils des hommes.
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 Car 1 000 ans, à tes yeux, sont comme le jour d’hier quand il est passé, et comme une veille dans la nuit.
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 Comme un torrent tu les emportes; ils sont comme un sommeil, – au matin, comme l’herbe qui reverdit:
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 Au matin, elle fleurit et reverdit; le soir on la coupe, et elle sèche.
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
7 Car nous sommes consumés par ta colère, et nous sommes épouvantés par ta fureur.
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
8 Tu as mis devant toi nos iniquités, devant la lumière de ta face nos [fautes] cachées.
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
9 Car tous nos jours s’en vont par ta grande colère; nous consumons nos années comme une pensée.
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 Les jours de nos années montent à 70 ans, et si, à cause de la vigueur, ils vont à 80 ans, leur orgueil encore est peine et vanité; car [notre vie] s’en va bientôt, et nous nous envolons.
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
11 Qui connaît la force de ta colère, et, selon ta crainte, ton courroux?
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 Enseigne-nous ainsi à compter nos jours, afin que nous en acquérions un cœur sage.
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
13 Éternel! retourne-toi. – Jusques à quand? – Et repens-toi à l’égard de tes serviteurs.
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Rassasie-nous, au matin, de ta bonté; et nous chanterons de joie, et nous nous réjouirons tous nos jours.
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Réjouis-nous selon les jours où tu nous as affligés, selon les années où nous avons vu des maux.
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Que ton œuvre apparaisse à tes serviteurs, et ta majesté à leurs fils.
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
17 Et que la gratuité du Seigneur, notre Dieu, soit sur nous; et établis sur nous l’œuvre de nos mains: oui, l’œuvre de nos mains, établis-la.
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

< Psaumes 90 >