< Psaumes 82 >
1 Psaume d’Asaph. Dieu se tient dans l’assemblée de Dieu; il juge au milieu des juges.
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 Jusques à quand jugerez-vous injustement et ferez-vous acception de la personne des méchants? (Sélah)
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3 Faites droit au misérable et à l’orphelin, faites justice à l’affligé et au nécessiteux.
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Délivrez le misérable et le pauvre, sauvez-le de la main des méchants.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 Ils ne connaissent ni ne comprennent, ils marchent dans les ténèbres: tous les fondements de la terre chancellent.
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 Moi j’ai dit: Vous êtes des dieux, et vous êtes tous fils du Très-haut.
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Mais vous mourrez comme un homme, et vous tomberez comme un des princes.
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Lève-toi, ô Dieu! juge la terre; car tu hériteras toutes les nations.
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.