< Psaumes 77 >

1 Au chef de musique. Sur Jeduthun. D’Asaph. Psaume. Ma voix s’adresse à Dieu, et je crierai; ma voix s’adresse à Dieu, et il m’écoutera.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
2 Au jour de ma détresse j’ai cherché le Seigneur; ma main était étendue durant la nuit et ne se lassait point; mon âme refusait d’être consolée.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
3 Je me souvenais de Dieu, et j’étais agité; je me lamentais, et mon esprit défaillait. (Sélah)
Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
4 Tu tiens ouvertes mes paupières; je suis inquiet, et je ne parle pas.
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
5 Je pense aux jours d’autrefois, aux années des siècles passés.
Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
6 Je me souviens, de nuit, de mon cantique; je médite en mon cœur, et mon esprit cherche diligemment.
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
7 Le Seigneur rejettera-t-il pour toujours? et ne montrera-t-il plus sa faveur?
“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
8 Sa bonté a-t-elle cessé pour toujours? Sa parole a-t-elle pris fin de génération en génération?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
9 Dieu a-t-il oublié d’user de grâce? A-t-il enfermé ses miséricordes dans la colère? (Sélah)
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
10 Et je dis: C’est ici mon infirmité; – [je me souviendrai des] années de la droite du Très-haut,
Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Je me souviendrai des œuvres de Jah; car je me souviendrai de tes merveilles d’autrefois,
Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Et je penserai à toute ton œuvre, et je méditerai tes actes.
Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
13 Ô Dieu! ta voie est dans le lieu saint. Où y a-t-il un dieu grand comme Dieu?
Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Toi, tu es le Dieu qui fais des merveilles; tu as fait connaître ta puissance parmi les peuples.
Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Tu as racheté par [ton] bras ton peuple, les fils de Jacob et de Joseph. (Sélah)
Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
16 Les eaux t’ont vu, ô Dieu! les eaux t’ont vu, elles ont tremblé; les abîmes aussi se sont émus.
Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
17 Les nuées ont versé des eaux, les nuages ont fait retentir une voix, et tes flèches se sont promenées.
Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 La voix de ton tonnerre était dans le tourbillon, les éclairs ont illuminé le monde; la terre en a été émue et a tremblé.
Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Ta voie est dans la mer, et tes sentiers dans les grandes eaux; et tes traces ne sont pas connues.
Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
20 Tu as conduit ton peuple comme un troupeau, par la main de Moïse et d’Aaron.
Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

< Psaumes 77 >