< Psaumes 73 >

1 Psaume d’Asaph. Certainement Dieu est bon envers Israël, envers ceux qui sont purs de cœur.
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 Et pour moi, il s’en est fallu de peu que mes pieds ne m’aient manqué, – d’un rien que mes pas n’aient glissé;
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 Car j’ai porté envie aux arrogants, en voyant la prospérité des méchants.
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 Car [il n’y a] pas de tourments dans leur mort, et leur corps est gras;
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 Ils n’ont point de part aux peines des humains, et ils ne sont pas frappés avec les hommes.
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 C’est pourquoi l’orgueil les entoure comme un collier, la violence les couvre comme un vêtement;
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 Les yeux leur sortent de graisse; ils dépassent les imaginations de leur cœur.
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 Ils sont railleurs et parlent méchamment d’opprimer; ils parlent avec hauteur;
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 Ils placent leur bouche dans les cieux, et leur langue se promène sur la terre.
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 C’est pourquoi son peuple se tourne de ce côté-là, et on lui verse l’eau à plein bord,
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 Et ils disent: Comment Dieu connaîtrait-il, et y aurait-il de la connaissance chez le Très-haut?
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Voici, ceux-ci sont des méchants, et ils prospèrent dans le monde, ils augmentent leurs richesses.
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Certainement c’est en vain que j’ai purifié mon cœur et que j’ai lavé mes mains dans l’innocence:
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 J’ai été battu tout le jour, et mon châtiment [revenait] chaque matin.
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 Si j’avais dit: Je parlerai ainsi, voici, j’aurais été infidèle à la génération de tes fils.
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 Quand j’ai médité pour connaître cela, ce fut un travail pénible à mes yeux,
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 Jusqu’à ce que je sois entré dans les sanctuaires de Dieu…: j’ai compris leur fin.
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Certainement tu les places en des lieux glissants, tu les fais tomber en ruines.
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Comme ils sont détruits en un moment! Ils sont péris, consumés par la frayeur.
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 Comme un songe, quand on s’éveille, tu mépriseras, Seigneur, leur image, lorsque tu t’éveilleras.
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 Quand mon cœur s’aigrissait, et que je me tourmentais dans mes reins,
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 J’étais alors stupide et je n’avais pas de connaissance; j’étais avec toi comme une brute.
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 Mais je suis toujours avec toi: tu m’as tenu par la main droite;
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Tu me conduiras par ton conseil, et, après la gloire, tu me recevras.
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Qui ai-je dans les cieux? Et je n’ai eu de plaisir sur la terre qu’en toi.
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 Ma chair et mon cœur sont consumés; Dieu est le rocher de mon cœur, et mon partage pour toujours.
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 Car voici, ceux qui sont loin de toi périront; tu détruiras tous ceux qui se prostituent en se détournant de toi.
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 Mais, pour moi, m’approcher de Dieu est mon bien; j’ai mis ma confiance dans le Seigneur, l’Éternel, pour raconter tous tes faits.
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

< Psaumes 73 >