< Psaumes 70 >
1 Au chef de musique. De David; pour faire souvenir. Hâte-toi, ô Dieu, de me délivrer! [hâte-toi], ô Éternel, de me secourir!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2 Que ceux qui cherchent ma vie soient honteux et confondus; qu’ils se retirent en arrière et soient confus, ceux qui prennent plaisir à mon malheur;
Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
3 Qu’ils retournent en arrière à cause de leur honte, ceux qui disent: Ha ha! ha ha!
Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4 Que tous ceux qui te cherchent s’égaient et se réjouissent en toi; et que ceux qui aiment ton salut disent continuellement: Magnifié soit Dieu!
Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5 Et moi, je suis affligé et pauvre; ô Dieu, hâte-toi vers moi! Tu es mon secours et celui qui me délivre; Éternel, ne tarde pas!
Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.