< Psaumes 63 >
1 Psaume de David; quand il était dans le désert de Juda. Ô Dieu! tu es mon Dieu; je te cherche au point du jour; mon âme a soif de toi, ma chair languit après toi, dans une terre aride et altérée, sans eau,
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 Pour voir ta force et ta gloire, comme je t’ai contemplé dans le lieu saint.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Car ta bonté est meilleure que la vie; mes lèvres te loueront.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Ainsi je te bénirai durant ma vie, j’élèverai mes mains en ton nom.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 Mon âme est rassasiée comme de moelle et de graisse, et ma bouche [te] louera avec des lèvres qui chantent de joie.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 Quand je me souviens de toi sur mon lit, je médite de toi durant les veilles de la nuit;
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Car tu as été mon secours, et à l’ombre de tes ailes je chanterai de joie.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Mon âme s’attache à toi pour te suivre, ta droite me soutient.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Mais ceux qui cherchent ma vie pour sa ruine entreront dans les parties inférieures de la terre;
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 On les livrera à la puissance de l’épée, ils seront la portion des renards.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 Mais le roi se réjouira en Dieu, [et] quiconque jure par lui se glorifiera; car la bouche de ceux qui parlent faussement sera fermée.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.