< Psaumes 58 >

1 Au chef de musique. Al-Tashkheth. De David. Mictam. Est-ce que vraiment la justice se tait? Prononcez-vous [ce qui est juste]? Vous, fils des hommes, jugez-vous avec droiture?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Bien plutôt, dans le cœur, vous commettez des iniquités; dans le pays, vous pesez la violence de vos mains.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Les méchants se sont égarés dès la matrice; ils errent dès le ventre, parlant le mensonge.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Ils ont un venin semblable au venin d’un serpent, comme l’aspic sourd qui se bouche l’oreille,
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Qui n’entend pas la voix des charmeurs, du sorcier expert en sorcelleries.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Ô Dieu! dans leur bouche brise leurs dents; Éternel! arrache les grosses dents des jeunes lions.
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Qu’ils se fondent comme des eaux qui s’écoulent! S’il ajuste ses flèches, qu’elles soient comme cassées!
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Qu’ils soient comme une limace qui va se fondant! Comme l’avorton d’une femme, qu’ils ne voient pas le soleil!
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Avant que vos chaudières aient senti les épines, vertes ou enflammées, le tourbillon les emportera.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Le juste se réjouira quand il verra la vengeance; il lavera ses pieds dans le sang du méchant.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Et l’homme dira: Certainement il y a un fruit pour le juste, certainement il y a un Dieu qui juge sur la terre.
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

< Psaumes 58 >