< Psaumes 55 >

1 Au chef de musique. Sur Neguinoth; pour instruire. De David. Prête l’oreille, ô Dieu, à ma prière, et ne te cache pas de ma supplication.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
2 Écoute-moi, et réponds-moi; je m’agite dans ma plainte et je me lamente,
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 À cause de la voix de l’ennemi [et] devant l’oppression du méchant; car ils font tomber sur moi l’iniquité, et me poursuivent avec passion.
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 Mon cœur est dans l’angoisse au-dedans de moi, et des frayeurs mortelles sont tombées sur moi;
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
5 La crainte et le tremblement sont venus sur moi, et un frisson de terreur m’a couvert.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 Et j’ai dit: Oh! si j’avais des ailes comme une colombe, je m’envolerais et je demeurerais tranquille;
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 Voici, je m’enfuirais loin, et je me logerais au désert. (Sélah)
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
8 Je me hâterais de m’échapper loin du vent de tempête, loin de l’ouragan.
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 Engloutis-[les], Seigneur! divise leur langue; car j’ai vu la violence et les querelles dans la ville.
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Jour et nuit ils font la ronde sur ses murailles; et l’iniquité et le tourment sont au milieu d’elle;
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 La perversité est au milieu d’elle, et l’oppression et la fraude ne s’éloignent pas de ses places.
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 Car ce n’est pas un ennemi qui m’a outragé, alors je l’aurais supporté; ce n’est point celui qui me hait qui s’est élevé orgueilleusement contre moi, alors je me serais caché de lui;
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
13 Mais c’est toi, un homme comme moi, mon conseiller et mon ami:
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Nous avions ensemble de douces communications; nous allions avec la foule dans la maison de Dieu.
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 Que la mort les saisisse! qu’ils descendent vivants dans le shéol! Car la malice est dans leur demeure, au milieu d’eux. (Sheol h7585)
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
16 Moi, je crie à Dieu; et l’Éternel me sauvera.
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Le soir, et le matin, et à midi, je médite et je me lamente; et il entendra ma voix.
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
18 Il a mis en paix mon âme, la rachetant de la guerre qu’on me fait, car ils étaient plusieurs autour de moi.
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 Dieu a entendu, et il les accablera: il demeure dès les jours d’autrefois; (Sélah) car il n’y a point de changement en eux, et ils ne craignent pas Dieu.
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
20 [Le méchant] a étendu ses mains sur ceux qui sont en paix avec lui; il a profané son alliance.
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
21 [Les paroles de] sa bouche étaient lisses comme le beurre, mais la guerre était dans son cœur; ses paroles étaient douces comme l’huile, mais elles sont des épées nues.
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22 Rejette ton fardeau sur l’Éternel, et il te soutiendra; il ne permettra jamais que le juste soit ébranlé.
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 Et toi, ô Dieu! tu les feras descendre dans le puits de la destruction: les hommes de sang et de fourbe n’atteindront pas la moitié de leurs jours; mais moi, je me confierai en toi.
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.

< Psaumes 55 >