< Psaumes 53 >

1 Au chef de musique. Sur Mahalath; pour instruire. De David. L’insensé a dit dans son cœur: Il n’y a point de Dieu. Ils se sont corrompus, et ils ont rendu abominable la perversité; il n’y a personne qui fasse le bien.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2 Dieu a regardé des cieux sur les fils des hommes, pour voir s’il y a quelqu’un qui soit intelligent, qui recherche Dieu:
Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
3 Ils se sont tous retirés, ils se sont tous ensemble corrompus; il n’y a personne qui fasse le bien, non pas même un seul.
Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
4 Les ouvriers d’iniquité n’ont-ils aucune connaissance? Ils dévorent mon peuple, comme on mange du pain; ils n’invoquent point Dieu.
Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5 Là où il n’y avait pas de sujet de frayeur ils ont été saisis de frayeur; car Dieu disperse les os de ceux qui se campent contre toi. Tu les as rendus confus, parce que Dieu les a méprisés.
Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6 Oh! si de Sion le salut d’Israël était venu! Quand Dieu rétablira les captifs de son peuple, Jacob s’égaiera, Israël se réjouira.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

< Psaumes 53 >