< Psaumes 49 >
1 Au chef de musique. Des fils de Coré. Psaume. Vous, tous les peuples, entendez ceci; vous, tous les habitants du monde, prêtez l’oreille;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 Fils des gens du commun, et fils des grands, le riche et le pauvre pareillement:
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 Ma bouche dira des paroles de sagesse, et la méditation de mon cœur sera [pleine] d’intelligence;
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 Je prêterai l’oreille au discours sentencieux, j’exposerai mon énigme sur la harpe.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Pourquoi craindrais-je au mauvais jour, quand l’iniquité de ceux qui me talonnent m’enveloppe?
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 Ils se confient en leurs biens et se glorifient en l’abondance de leurs richesses…
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 Un homme ne pourra en aucune manière racheter son frère, ni donner à Dieu sa rançon,
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 (Car précieux est le rachat de leur âme, et il faut qu’il y renonce à jamais, )
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 Afin qu’il vive encore, à toujours, [et] qu’il ne voie pas la fosse.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 Car il voit que les sages meurent, que le sot et l’insensé périssent pareillement et laissent leurs biens à d’autres.
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 Leur [pensée] intérieure est que leurs maisons durent à toujours, et leurs demeures de génération en génération; ils appellent les terres de leur propre nom.
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 Pourtant l’homme qui est en honneur ne dure pas; il est semblable aux bêtes qui périssent.
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 Ce chemin qu’ils tiennent est leur folie; mais ceux qui viennent après eux prennent plaisir aux propos de leur bouche. (Sélah)
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 Ils gisent dans le shéol comme des brebis: la mort se repaît d’eux, et au matin les hommes droits domineront sur eux; et leur beauté va se consumer dans le shéol, sans qu’ils aient plus de demeure. (Sheol )
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
15 Mais Dieu rachètera mon âme de la puissance du shéol, car il me prendra. (Sélah) (Sheol )
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
16 Ne crains pas quand un homme s’enrichit, quand la gloire de sa maison s’accroît;
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 Car, lorsqu’il mourra, il n’emportera rien; sa gloire ne descendra pas après lui,
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 Quoique pendant sa vie il bénisse son âme (et on te louera, si tu te fais du bien),
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 Il s’en ira jusqu’à la génération de ses pères: ils ne verront jamais la lumière.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 L’homme qui est en honneur et n’a point d’intelligence, est comme les bêtes qui périssent.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.