< Psaumes 147 >

1 Louez Jah! car c’est une chose bonne. Chantez les louanges de notre Dieu! car c’est une chose agréable. La louange est bienséante.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 L’Éternel bâtit Jérusalem; il rassemble les exilés d’Israël.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 C’est lui qui guérit ceux qui ont le cœur brisé, et qui bande leurs plaies;
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 Qui compte le nombre des étoiles: à elles toutes il donne des noms.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Notre Seigneur est grand et d’une grande puissance; son intelligence est sans bornes.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 L’Éternel affermit les débonnaires; il renverse les méchants jusqu’en terre.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Chantez à l’Éternel avec actions de grâces, psalmodiez sur la harpe à notre Dieu,
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Qui couvre de nuages les cieux, qui prépare la pluie pour la terre, qui fait germer l’herbe sur les montagnes;
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Qui donne la nourriture au bétail, [et] aux petits du corbeau qui crient.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 Il ne trouve pas son plaisir en la force du cheval, il ne se complaît pas aux jambes de l’homme.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 Le plaisir de l’Éternel est en ceux qui le craignent, en ceux qui s’attendent à sa bonté.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Jérusalem, célèbre l’Éternel! Sion, loue ton Dieu!
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 Car il rend fortes les barres de tes portes; il bénit tes fils au milieu de toi;
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 Il met la paix dans tes confins; il te rassasie de la moelle du froment;
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 Il envoie ses oracles sur la terre: sa parole court avec vitesse.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 C’est lui qui donne la neige comme de la laine, qui répand la gelée blanche comme de la cendre;
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 Il jette sa glace comme par morceaux: qui peut subsister devant son froid?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Il envoie sa parole et les fait fondre; il fait souffler son vent: les eaux coulent.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 Il annonce ses paroles à Jacob, ses statuts et ses ordonnances à Israël.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 Il n’a fait ainsi à aucune nation; et ses ordonnances, elles ne les ont pas connues. Louez Jah!
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psaumes 147 >