< Psaumes 138 >

1 De David. Je te célébrerai de tout mon cœur; je chanterai tes louanges devant les dieux.
Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
2 Je me prosternerai vers le temple de ta sainteté, et je célébrerai ton nom à cause de ta bonté et à cause de ta vérité; car tu as exalté ta parole au-dessus de tout ton nom.
Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
3 Au jour où j’ai crié, tu m’as répondu; tu as augmenté la force de mon âme.
Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
4 Tous les rois de la terre te célébreront, ô Éternel! quand ils auront entendu les paroles de ta bouche;
Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
5 Et ils chanteront dans les voies de l’Éternel, car grande est la gloire de l’Éternel.
Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6 Car l’Éternel est haut élevé; mais il voit ceux qui sont en bas état, et il connaît de loin les hautains.
Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
7 Si je marche au milieu de la détresse, tu me feras vivre, tu étendras ta main contre la colère de mes ennemis, et ta droite me sauvera.
Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
8 L’Éternel achèvera ce qui me concerne. Éternel! ta bonté demeure à toujours. N’abandonne pas les œuvres de tes mains.
Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.

< Psaumes 138 >