< Psaumes 122 >
1 Cantique des degrés. De David. Je me suis réjoui quand ils m’ont dit: Allons à la maison de l’Éternel!
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 Nos pieds se tiendront dans tes portes, ô Jérusalem!
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 Jérusalem, qui es bâtie comme une ville bien unie ensemble en elle-même!
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 C’est là que montent les tribus, les tribus de Jah, un témoignage à Israël, pour célébrer le nom de l’Éternel.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 Car là sont placés les trônes de jugement, les trônes de la maison de David.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 Demandez la paix de Jérusalem; ceux qui t’aiment prospéreront.
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 Que la paix soit dans tes murs, la prospérité dans tes palais!
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 À cause de mes frères et de mes compagnons, je dirai: Que la paix soit en toi!
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 À cause de la maison de l’Éternel, notre Dieu, je rechercherai ton bien.
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.