< Psaumes 103 >
1 De David. Mon âme, bénis l’Éternel! Et que tout ce qui est au-dedans de moi, [bénisse] son saint nom!
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 Mon âme, bénis l’Éternel, et n’oublie aucun de ses bienfaits.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 C’est lui qui pardonne toutes tes iniquités, qui guérit toutes tes infirmités,
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 Qui rachète ta vie de la fosse, qui te couronne de bonté et de compassions,
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 Qui rassasie de biens ta vieillesse; ta jeunesse se renouvelle comme celle de l’aigle.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 L’Éternel fait justice et droit à tous les opprimés.
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 Il a fait connaître ses voies à Moïse, ses actes aux fils d’Israël.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 L’Éternel est miséricordieux, et plein de grâce, lent à la colère et d’une grande bonté.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 Il ne contestera pas à jamais, et il ne garde pas sa colère à toujours.
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 Il ne nous a pas fait selon nos péchés, et ne nous a pas rendu selon nos iniquités.
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 Car comme les cieux sont élevés au-dessus de la terre, sa bonté est grande envers ceux qui le craignent.
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 Autant l’orient est loin de l’occident, autant il a éloigné de nous nos transgressions.
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 Comme un père a compassion de ses fils, l’Éternel a compassion de ceux qui le craignent.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 Car il sait de quoi nous sommes formés, il se souvient que nous sommes poussière.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 L’homme, … ses jours sont comme l’herbe; il fleurit comme la fleur des champs;
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 Car le vent passe dessus, et elle n’est plus, et son lieu ne la reconnaît plus.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 Mais la bonté de l’Éternel est de tout temps et à toujours sur ceux qui le craignent, et sa justice pour les fils de leurs fils,
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 Pour ceux qui gardent son alliance, et qui se souviennent de ses préceptes pour les faire.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 L’Éternel a établi son trône dans les cieux, et son royaume domine sur tout.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Bénissez l’Éternel, vous, ses anges puissants en force, qui exécutez sa parole, écoutant la voix de sa parole!
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Bénissez l’Éternel, vous, toutes ses armées, qui êtes ses serviteurs, accomplissant son bon plaisir!
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Bénissez l’Éternel, vous, toutes ses œuvres, dans tous les lieux de sa domination! Mon âme, bénis l’Éternel!
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.